Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




1 Samueli 2:7 - Buku Lopatulika

Yehova asaukitsa, nalemeretsa; achepetsa, nakuzanso.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Yehova asaukitsa, nalemeza; achepetsa, nakuzanso.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Chauta amasaukitsa ndipo amalemeretsa, amatsitsa ndipo amakweza.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yehova amasaukitsa ndipo amalemeretsa, amatsitsa ndipo amakweza.

Onani mutuwo



1 Samueli 2:7
17 Mawu Ofanana  

Nanyamuka, nalowa m'nyumba; ndipo anatsanulira mafutawo pamutu pake, nanena naye, Atero Yehova Mulungu wa Israele, Ndakudzoza ukhale mfumu ya pa anthu a Yehova, ndiwo Aisraele.


Zolemera ndi ulemu zifuma kwanu, ndipo muchita ufumu pa zonse, ndi m'dzanja mwanu muli mphamvu yaikulu; kukuza ndi kupatsa onse mphamvu kuli m'dzanja lanu.


Ndipo chuma ndi ulemu zinachulukira Hezekiya, nadzimangira iye zosungiramo siliva, ndi golide, ndi timiyala ta mtengo wake, ndi zonunkhira, ndi zikopa, ndi zipangizo zokoma zilizonse;


Nadzimangiranso mizinda, nadzionera nkhosa ndi ng'ombe zochuluka; pakuti Mulungu adampatsa chuma chambirimbiri.


nati, Ndinatuluka m'mimba ya mai wanga wamaliseche, wamaliseche ndidzamukanso; Yehova anapatsa, Yehova watenga, lidalitsike dzina la Yehova.


Upenyerere aliyense wodzikuza, numtsitse, nupondereze oipa pomwe akhala.


kuika opeputsidwa pamalo ponyamuka, kuti iwo a maliro akwezedwe kosatekeseka.


chifukwa cha ukali wanu ndi kuzaza kwanu; popeza munandinyamula ndipo munandigwetsa.


Pakuti Mulungu ndiye woweruza; achepsa wina, nakuza wina.


Pakuti m'dzanja la Yehova muli chikho; ndi vinyo wake achita thovu; chidzala ndi zosakanizira, ndipo atsanulako. Indedi, oipa onse a padziko lapansi adzamwa nadzagugudiza nsenga zake.


Wolemera ndi wosauka akumana, wolenga onsewo ndiye Yehova.


Chifukwa padzakhala tsiku la Yehova wa makamu pa zonse zonyada ndi zakudzikuza, ndi pa zonse zotukulidwa; ndipo zidzatsitsidwa;


Pakuti, taona, ndakuyesa iwe wamng'ono mwa amitundu, ndi wonyozedwa mwa anthu.


Ndipo mitengo yonse yakuthengo idzadziwa kuti Ine Yehova ndatsitsa mtengo wosomphoka, ndakuza mtengo waung'ono, ndaumitsa mtengo wauwisi, ndi kuphukitsa mtengo wouma; Ine Yehova ndanena ndi kuchichita.


Dzichepetseni pamaso pa Ambuye, ndipo adzakukwezani.