Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa

Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano


Masalimo 20 - Buku Lopatulika Buku Lopatulika
Masalimo 20

Kupempherera mfumu potulukira iye kunkhondo
Kwa Mkulu wa Nyimbo. Salimo la Davide.

1 Yehova akuvomereze tsiku la nsautso; dzina la Mulungu wa Yakobo likuike pamsanje;

2 likutumizire thandizo lotuluka m'malo oyera, ndipo likugwirizize kuchokera mu Ziyoni;

3 likumbukire zopereka zako zonse, lilandire nsembe yako yopsereza;

4 likupatse cha mtima wako, ndipo likwaniritse upo wako wonse.

5 Tidzafuula mokondwera mwa chipulumutso chanu, ndipo m'dzina la Mulungu wathu tidzakweza mbendera; Yehova akwaniritse mapempho ako onse.

6 Tsopano ndidziwa kuti Yehova apulumutsa wodzozedwa wake; adzamvomereza mu Mwamba mwake moyera ndi mphamvu ya chipulumutso cha dzanja lake lamanja.

7 Ena atama magaleta, ndi ena akavalo; koma ife tidzatchula dzina la Yehova Mulungu wathu.

8 Iwowa anagonjeka, nagwa; koma ife tauka, ndipo takhala chilili.

9 Yehova, pulumutsani, mfumuyo ativomereze tsiku lakuitana ife.

Bible Society of Malawi

Bible Society of Malawi