Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa

Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano


Masalimo 124 - Buku Lopatulika Buku Lopatulika
Masalimo 124

Mulungu yekha walanditsa anthu ake
Nyimbo yokwerera; ya Davide.

1 Akadapanda kukhala nafe Yehova, anene tsono Israele;

2 Akadapanda kukhala nafe Yehova, pakutiukira anthu:

3 Akadatimeza amoyo, potipsera mtima wao.

4 Akadatimiza madziwo, mtsinje ukadapita pa moyo wathu;

5 madzi odzikuza akadapita pa moyo wathu.

6 Alemekezedwe Yehova, amene sanatipereke kumano kwao tikhale chakudya chao.

7 Moyo wathu unaonjoka ngati mbalame mu msampha wa msodzi; msampha unathyoka ndi ife tinaonjoka.

8 Thandizo lathu lili m'dzina la Yehova, wolenga kumwamba ndi dziko lapansi.

Bible Society of Malawi

Bible Society of Malawi