Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -

Masalimo 114 - Buku Lopatulika


Alemekeze Mulungu pa chipulumutso chija cha mu Ejipito

1 M'mene Israele anatuluka ku Ejipito, nyumba ya Yakobo kwa anthu a chinenedwe chachilendo;

2 Yuda anakhala malo ake oyera, Israele ufumu wake.

3 Nyanjayo inaona, nithawa; Yordani anabwerera m'mbuyo.

4 Mapiri anatumphatumpha ngati nkhosa zamphongo, timapiri ngati anaankhosa.

5 Unathawanji nawe, nyanja iwe? Unabwereranji m'mbuyo, Yordani iwe?

6 Munatumphatumphiranji ngati nkhosa zamphongo, mapiri inu? Ngati anaankhosa, zitunda inu?

7 Unjenjemere, dziko lapansi iwe, pamaso pa Ambuye, pamaso pa Mulungu wa Yakobo;

8 amene anasanduliza thanthwe likhale thawale lamadzi, nsangalabwi ikhale kasupe wamadzi.

Bible Society of Malawi

Bible Society of Malawi
Titsatireni:



Zotsatsa