Ndipo pamene Iye anawauza makamuwo, anakwera m'phiri pa yekha, kukapemphera: ndipo pamene panali madzulo, Iye anakhala kumeneko yekha.
Yohane 6:3 - Buku Lopatulika Koma Yesu anakwera kuphiri, nakhala pansi komweko pamodzi ndi ophunzira ake. Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014 Koma Yesu anakwera kuphiri, nakhala pansi komweko pamodzi ndi ophunzira ake. Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa Yesu adakwera m'phiri nakhala pansi ndi ophunzira ake. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Kenaka Yesu anakwera pa phiri nakhala pansi ndi ophunzira ake. |
Ndipo pamene Iye anawauza makamuwo, anakwera m'phiri pa yekha, kukapemphera: ndipo pamene panali madzulo, Iye anakhala kumeneko yekha.
Ndipo Yesu anachoka kumeneko, nadza kunyanja ya Galileya, nakwera m'phiri, nakhala pansi pamenepo.
Ndipo m'mene Iye anaona makamu, anakwera m'phiri; ndipo m'mene Iye anakhala pansi, anadza kwa Iye ophunzira ake;
Ndipo anakwera m'phiri, nadziitanira iwo amene anawafuna Iye mwini; ndipo anadza kwa Iye.
Ndipo pamene padatha ngati masiku asanu ndi atatu atanena mau amenewa, Iye anatenga Petro ndi Yohane ndi Yakobo apite naye, nakwera m'phiri kukapemphera.
Pamenepo Yesu, pozindikira kuti alikufuna kudza kudzamgwira Iye, kuti amlonge ufumu, anachokanso kunka kuphiri pa yekha.