Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti

- Zotsatsa -




Luka 9:28 - Buku Lopatulika

28 Ndipo pamene padatha ngati masiku asanu ndi atatu atanena mau amenewa, Iye anatenga Petro ndi Yohane ndi Yakobo apite naye, nakwera m'phiri kukapemphera.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

28 Ndipo pamene padatha ngati masiku asanu ndi atatu atanena mau amenewa, Iye anatenga Petro ndi Yohane ndi Yakobo apite naye, nakwera m'phiri kukapemphera.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

28 Patapita ngati masiku asanu ndi atatu atanena mau ameneŵa, Yesu adatenga Petro, Yohane ndi Yakobe, nakwera nawo ku phiri kukapemphera.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

28 Patatha pafupifupi masiku asanu ndi atatu Yesu atanena izi, Iye anatenga Petro, Yohane ndi Yakobo ndi kukwera ku phiri kukapemphera.

Onani mutuwo Koperani




Luka 9:28
18 Mawu Ofanana  

M'malo mwa chikondi changa andibwezera udani; koma ine, kupemphera ndiko.


Ndipo pamene Iye anawauza makamuwo, anakwera m'phiri pa yekha, kukapemphera: ndipo pamene panali madzulo, Iye anakhala kumeneko yekha.


Ndipo m'mene Iye anaona makamu, anakwera m'phiri; ndipo m'mene Iye anakhala pansi, anadza kwa Iye ophunzira ake;


Ndipo m'mawa mwake anauka usikusiku, natuluka namuka kuchipululu, napemphera kumeneko.


Ndipo atalawirana nao, anachoka Iye, nalowa m'phiri kukapemphera.


Pamene anthu onse anabatizidwa, Yesu nayenso anabatizidwa. Iye anali kupemphera, ndipo kuthambo kunatseguka,


Koma Iye anazemba, nanka m'mapululu, nakapemphera.


Ndipo kunali masiku awa, Iye anatuluka nanka kuphiri kukapemphera; nachezera usiku wonse m'kupemphera kwa Mulungu.


Ndipo pakufika Iye kunyumbako, sanaloleze wina kulowa naye pamodzi, koma Petro, ndi Yohane, ndi Yakobo, ndi atate wa mwanayo, ndi amake.


Ndipo kunali, pamene Iye anali kupemphera padera, ophunzira anali naye; ndipo anawafunsa iwo, kuti, Makamuwo a anthu anena kuti Ine ndine yani?


Koma Yesu anakwera kuphiri, nakhala pansi komweko pamodzi ndi ophunzira ake.


Nthawi yachitatu iyi ndilinkudza kwa inu. Pakamwa pa mboni ziwiri kapena zitatu maneno onse adzakhazikika.


Ameneyo, m'masiku a thupi lake anapereka mapemphero ndi mapembedzero pamodzi ndi kulira kwakukulu ndi misozi kwa Iye amene anakhoza kumpulumutsa Iye muimfa, ndipo anamveka popeza anaopa Mulungu,


Pakuti sitinatsate miyambi yachabe, pamene tinakudziwitsani mphamvu ndi maonekedwe a Ambuye wathu Yesu Khristu, koma tinapenya m'maso ukulu wake.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa