Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Yohane 16:4 - Buku Lopatulika

Koma zinthu izi ndalankhula ndi inu kuti ikadza nthawi yao, mukakumbukire kuti ndinakuuzani. Koma izi sindinanene kwa inu kuyambira pachiyambi, chifukwa ndinali pamodzi ndi inu.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Koma zinthu izi ndalankhula ndi inu kuti ikadza nthawi yao, mukakumbukire kuti ndinakuuzani. Koma izi sindinanena kwa inu kuyambira pachiyambi, chifukwa ndinali pamodzi ndi inu.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Koma ndimati muzimve zimenezi kuti nthaŵi yakeyo ikadzafika, mudzakumbukire kuti ndidaakuuziranitu.” “Sindidakuuzeni zimenezi poyamba paja ai, chifukwa ndinali nanu pamodzi.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Ine ndakuwuzani izi kuti nthawi ikadzafika mudzakumbukire kuti Ine ndinakuchenjezani kale. Ine sindinakuwuzeni izi poyamba paja chifukwa ndinali nanu.”

Onani mutuwo



Yohane 16:4
15 Mawu Ofanana  

Ndipo pamene mulikupita lalikani kuti, Ufumu wa Kumwamba wayandikira.


Chifukwa chake akanena kwa inu,


Ndipo Yesu anati kwa iwo, Nanga anyamata a nyumba ya ukwati angathe kulira kodi nthawi imene mkwati akhala nao? Koma adzafika masiku, pamene mkwati adzachotsedwa kwa iwo, ndipo pomwepo adzasala kudya.


Koma yang'anirani; onani ndakuuziranitu zinthu zonse, zisanafike.


Ndipo Yesu ananena nao, Kodi akhoza kusala kudya anyamata a ukwati pamene mkwati ali pamodzi nao? Pokhala ali naye mkwati pamodzi ndi iwo sangathe kusala.


monga anazipereka kwa ife iwo amene anakhala mboni ndi atumiki a mau,


Kuyambira tsopano ndinena kwa inu, chisadachitike, kuti pamene chitachitika, mukakhulupirire kuti ndine amene.


Ndipo tsopano ndakuuzani chisanachitike, kuti pamene chitachitika mukakhulupirire.


pakuti Ine ndidzamuonetsa iye zinthu zambiri ayenera iye kuzimva kuwawa chifukwa cha dzina langa.


Simukumbukira kodi, kuti pokhala nanu, ndisanachoke ine, ndinakuuzani izi?


podziwa kuti kuleka kwa msasa wanga kuli pafupi, monganso Ambuye wathu Yesu Khristu anandilangiza.