Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -




Yohane 16:3 - Buku Lopatulika

3 Ndipo izi adzachita, chifukwa sanadziwe Atate, kapena Ine.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

3 Ndipo izi adzachita, chifukwa sanadziwa Atate, kapena Ine.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

3 Adzachita zimenezi chifukwa sadadziŵe Atate kapenanso Ine.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

3 Iwo adzachita zoterozo chifukwa sanadziwe Atate kapena Inenso.

Onani mutuwo Koperani




Yohane 16:3
17 Mawu Ofanana  

Zonse zaperekedwa kwa Ine ndi Atate wanga; ndipo palibe munthu azindikira Mwana ali yani, koma Atate; ndipo Atate ali yani, koma Mwana, ndi iye amene Mwana afuna kumuululira Iye.


Koma izi zonse adzakuchitirani chifukwa cha dzina langa, chifukwa sadziwa wondituma Ine.


Iye wondida Ine, adanso Atate wanga.


Atate wolungama, dziko lapansi silinadziwe Inu, koma Ine ndinadziwa Inu; ndipo iwo anazindikira kuti munandituma Ine;


Koma moyo wosatha ndi uwu, kuti akadziwe Inu Mulungu woona yekha, ndi Yesu Khristu amene munamtuma.


Chifukwa chake ananena ndi Iye, Ali kuti Atate wanu? Yesu anayankha, Simudziwa kapena Ine, kapena Atate wanga; mukadadziwa Ine, mukadadziwanso Atate wanga.


ndipo inu simunamdziwe Iye; koma Ine ndimdziwa Iye; ndipo ngati ndinena kuti sindimdziwa Iye, ndidzakhala wonama chimodzimodzi inu; koma ndimdziwa Iye, ndipo ndisunga mau ake.


Ndipo tsopano, abale, ndidziwa kuti munachichita mosadziwa, monganso akulu anu.


imene saidziwa mmodzi wa akulu a nthawi ya pansi pano: pakuti akadadziwa sakadapachika Mbuye wa ulemerero;


m'lawi lamoto, ndi kubwezera chilango kwa iwo osamdziwa Mulungu, ndi iwo osamvera Uthenga Wabwino wa Ambuye wathu Yesu;


ndingakhale kale ndinali wamwano, ndi wolondalonda, ndi wachipongwe; komatu anandichitira chifundo, popeza ndinazichita wosazindikira, wosakhulupirira;


Yense wakukana Mwana, alibe Atate; wovomereza Mwana ali ndi Atatenso.


Taonani, chikondicho Atate watipatsa, kuti titchedwe ana a Mulungu; ndipo tili ife otere. Mwa ichi dziko lapansi silizindikira ife, popeza silimzindikira Iye.


Iye wosakonda sazindikira Mulungu; chifukwa Mulungu ndiye chikondi.


Ndipo tidziwa kuti Mwana wa Mulungu wafika, natipatsa ife chidziwitso, kuti tizindikire Woonayo, ndipo tili mwa Woonayo, mwa Mwana wake Yesu Khristu. Iye ndiye Mulungu woona ndi moyo wosatha.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa