Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Numeri 21:3 - Buku Lopatulika

Ndipo Yehova anamvera mau a Israele, napereka Akanani; ndipo anawaononga konse ndi mizinda yao yomwe; natcha dzina lake la malowo Horoma.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Ndipo Yehova anamvera mau a Israele, napereka Akanani; ndipo anawaononga konse ndi midzi yao yomwe; natcha dzina lake la malowo Horoma.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Chauta adamvera mau a Aisraelewo naŵaperekadi Akanani aja m'manja mwao. Aisraele adaŵaonongeratu Akananiwo pamodzi ndi mizinda yao yomwe. Choncho malowo adaŵatcha kuti Horoma.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yehova anamva pempho la Aisraeli ndipo anapereka Akanaaniwo kwa iwo. Anawawononga pamodzi ndi mizinda yawo. Kotero malowo anatchedwa Horima.

Onani mutuwo



Numeri 21:3
11 Mawu Ofanana  

Yehova, mwamva chikhumbo cha ozunzika, mudzakhazikitsa mtima wao, mudzatchereza khutu lanu;


anasamalira pemphero la iwo akusowa konse, osapepula pemphero lao.


Ndimkonda, popeza Yehova amamva mau anga ndi kupemba kwanga.


Adzandifuulira Ine ndipo ndidzamyankha; kunsautso ndidzakhala naye pamodzi; ndidzamlanditsa, ndi kumchitira ulemu.


Pamenepo anatsika Aamaleke, ndi Akanani, akukhala m'phirimo nawakantha, nawapha kufikira ku Horoma.


Ndipo Aamori, akukhala m'mapiri muja, anatuluka kukomana ndi inu, nakupirikitsani, monga zimachita njuchi, nakukanthani mu Seiri, kufikira ku Horoma.


Koma za mizinda ya amitundu awa, imene Yehova Mulungu wanu akupatsani, ikhale cholowa chanu, musasiyepo chamoyo chilichonse chakupuma;


mfumu ya ku Horoma, imodzi; mfumu ya ku Aradi, imodzi;


ndi Elitoladi, ndi Kesili ndi Horoma;


Ndipo Yuda anamuka ndi Simeoni mkulu wake, nakantha Akanani akukhala mu Zefati, nauononga konse. Koma dzina la mzindawo analitcha Horoma.


ndi kwa iwo a ku Horoma, ndi kwa iwo a ku Borasani, ndi kwa iwo a ku Ataki;