Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Masalimo 99:7 - Buku Lopatulika

Iye analankhula nao mu mtambo woti njo: Iwo anasunga mboni zake ndi malembawa anawapatsa.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Iye analankhula nao mu mtambo woti njo: Iwo anasunga mboni zake ndi malembawa anawapatsa.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Ankalankhula nawo mu mtambo woima kuti njo. Iwo ankasunga mapangano ndi malangizo amene Iye adaŵapatsa.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Iye anayankhula nawo kuchokera mʼchipilala cha mtambo; iwo anasunga malamulo ake ndi zophunzitsa zomwe anawapatsa.

Onani mutuwo



Masalimo 99:7
12 Mawu Ofanana  

Anatumiza mdima ndipo kunada; ndipo sanapikisane nao mau ake.


Ndipo Yehova anati kwa Mose, Taona, ndikudza kwa iwe mu mtambo wakuda bii, kuti anthu amve pamene ndilankhula ndi iwe, ndi kuti akuvomereze nthawi zonse. Pakuti Mose adauza Yehova mau a anthuwo.


Ndipo kunali, pakulowa Mose m'chihemacho, mtambo njo udafutsika, nuima pakhomo pa chihemacho; ndipo Yehova analankhula ndi Mose.


Anatero Mose; monga mwa zonse Yehova adamuuza, momwemo anachita.


Wopewetsa khutu lake kuti asamve chilamulo, ngakhale pemphero lake linyansa.


Ndipo Yehova anatsika mumtambo njo, naima pa khomo la chihema, naitana Aroni ndi Miriyamu; natuluka onse awiri.


Pamenepo Mose adapsa mtima, ndipo anati kwa Yehova, Musasamalira chopereka chao; sindinalande bulu wao mmodzi, kapena kuchitira choipa mmodzi wa iwowa.


amene anati za atate wake ndi amai wake, sindinamuone; Sanazindikire abale ake, sanadziwe ana ake omwe; popeza anasamalira mau anu, nasunga chipangano chanu.


Taonani, ndinakuphunzitsani malemba ndi maweruzo, monga Yehova Mulungu wanga anandiuza ine, kuti muzichita chotero pakati padziko limene munkako kulilandira likhale lanulanu.


amene anakhala wokhulupirika kwa Iye adamuikayo, monganso Mose m'nyumba yake yonse.