Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Masalimo 73:3 - Buku Lopatulika

Pakuti ndinachitira nsanje odzitamandira, pakuona mtendere wa oipa.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Pakuti ndinachitira nsanje odzitamandira, pakuona mtendere wa oipa.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Pakuti ndinkachita nsanje ndi anthu odzikuza, pamene ndidaona anthu oipa akulemera.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Pakuti ndinkachitira nsanje odzitamandira, pamene ndinaona mtendere wa anthu oyipa.

Onani mutuwo



Masalimo 73:3
14 Mawu Ofanana  

Mahema a achifwamba akhala mumtendere, ndi iwo oputa Mulungu alimbika mtima; amene Mulungu amadzazira dzanja lao.


Anthu oongoka mtima adzadabwa nacho, ndi munthu wosalakwa adzadziutsa kumtsutsa wonyoza Mulunguyo.


Oipa akhaliranji ndi moyo, nakalamba, nalemera kwakukulu?


Awalola akhale osatekeseka, ndipo alimbikapo; koma maso ake ali panjira zao.


Mayendedwe ake alimbika nthawi zonse; maweruzo anu ali pamwamba posaona iye; adani ake onse awanyodola.


Usavutike mtima chifukwa cha ochita zoipa, usachite nsanje chifukwa cha ochita chosalungama.


Khala chete mwa Yehova, numlindirire Iye; usavutike mtima chifukwa cha iye wolemerera m'njira yake, chifukwa cha munthu wakuchita chiwembu.


Mtima wako usachitire nsanje akuchimwawo; koma opabe Yehova tsiku lonse.


Usachitire nsanje anthu oipa, ngakhale kufuna kukhala nao;


Usachitire nsanje munthu wachiwawa; usasankhe njira yake iliyonse.


Ndaona zonsezi masiku anga achabe; pali wolungama angofa m'chilungamo chake, ndipo pali woipa angokhalabe ndi moyo m'kuipa kwake.


Wolungama ndinu, Yehova, pamene nditsutsana nanu mlandu; pokhapo ndinenane nanu za maweruzo; chifukwa chanji ipindula njira ya oipa? Chifukwa chanji akhala bwino onyengetsa?


Ndipo tsopano tiwatcha odzikuza odala, inde iwo ochita zoipa amangidwa ngati nyumba; inde, ayesa Mulungu, napulumuka.


Kodi muyesa kapena kuti malembo angonena chabe? Kodi Mzimuyo adamkhalitsa mwa ife akhumbitsa kuchita nsanje?