Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Masalimo 70:3 - Buku Lopatulika

Abwerere, kukhale mphotho ya manyazi ao amene akuti, Hede, hede.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Abwerere, kukhale mphotho ya manyazi ao amene akuti, Hede, hede.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Amene amandinyodola kuti, “Ha, Ha,” achoke ndi manyazi poona kuti alephera.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Onse amene akunena kwa ine kuti, “Aha, aha,” abwerere chifukwa cha manyazi awo.

Onani mutuwo



Masalimo 70:3
10 Mawu Ofanana  

Ndipo andiyasamira m'kamwa mwao; nati, Hede, Hede, diso lathu lidachipenya.


Asanene mumtima mwao, Hede, momwemo! Asanene, Tammeza iye.


Apululuke, mobwezera manyazi ao amene anena nane, Hede, hede.


Adani a moyo wanga achite manyazi, nathawe; chotonza ndi chimpepulo zikute ondifunira choipa.


Lilime langa lomwe lidzalankhula za chilungamo chanu tsiku lonse, pakuti ofuna kundichitira choipa achita manyazi, nadodoma.


nunene kwa ana a Amoni, Tamverani mau a Ambuye Yehova, Atero Ambuye Yehova, Popeza unati, Ha! Kunena malo anga opatulika; muja anadetsedwa ndi kunena dziko la Israele; muja linapasuka ndi kunena nyumba ya Yuda; muja adalowa kundende;


Wobadwa ndi munthu iwe, popeza Tiro ananyodola Yerusalemu, ndi kuti, Ha! Wathyoka uwu udali chipata cha mitundu ya anthu; wanditembenukira ine; ndidzakhuta ine, wapasuka uwu;


Atero Ambuye Yehova, Popeza mdani ananena za inu, Ha! Ingakhale misanje yakale ili yathu, cholowa chathu;


(Uyutu tsono anadzitengera kadziko ndi mphotho ya chosalungama; ndipo anagwa chamutu, naphulika pakati, ndi matumbo ake onse anakhuthuka;