Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -

Masalimo 70 - Buku Lopatulika


Davide apempha Mulungu amlanditse msanga
( Mas. 40.13-17 )
Kwa Mkulu wa Nyimbo. Salimo la Davide, la chikumbutso.

1 Fulumirani kundipulumutsa, Mulungu! Fulumirani kundithandiza, Yehova.

2 Achite manyazi, nadodome amene afuna moyo wanga. Abwezedwe m'mbuyo, napepulidwe amene akonda kundichitira choipa.

3 Abwerere, kukhale mphotho ya manyazi ao amene akuti, Hede, hede.

4 Asekerere nakondwerere mwa Inu onse akufuna Inu; nanene kosalekeza iwo akukonda chipulumutso chanu, abuke Mulungu.

5 Koma ine ndine wozunzika ndi waumphawi; mundifulumirire, Mulungu. Inu ndinu mthandizi wanga ndi Mpulumutsi wanga; musachedwe, Yehova.

Bible Society of Malawi

Bible Society of Malawi
Titsatireni:



Zotsatsa