Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Masalimo 141:3 - Buku Lopatulika

Muike mdindo pakamwa panga, Yehova; sungani pakhomo pa milomo yanga.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Muike mdindo pakamwa panga, Yehova; sungani pakhomo pa milomo yanga.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Muike mlonda pakamwa panga, Inu Chauta. Mulonde pa khomo la milomo yanga.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yehova ikani mlonda pakamwa panga; londerani khomo la pa milomo yanga.

Onani mutuwo



Masalimo 141:3
8 Mawu Ofanana  

Uletse lilime lako lisatchule zoipa, ndipo milomo yako isalankhule chinyengo.


Ndinati, Ndidzasunga njira zanga, kuti ndingachimwe ndi lilime langa. Ndidzasunga pakamwa panga ndi cham'kamwa, pokhala woipa ali pamaso panga.


Ndinatonthola osanena mau, ndinakhala chete osalawa chokoma; ndipo chisoni changa chinabuka.


M'kamwa mwanga mudzadzala lemekezo lanu, ndi ulemu wanu tsiku lonse.


Musakhulupirira bwenzi, musatama bwenzi loyanja; usamtsegulire pakhomo pakamwa pako, ngakhale kwa iye wogona m'fukato mwako.


Ngati wina adziyesera ali wopembedza Mulungu, ndiye wosamanga lilime lake, koma adzinyenga mtima wake, kupembedza kwake kwa munthuyu nkopanda pake.


Pakuti timakhumudwa tonse pa zinthu zambiri. Munthu akapanda kukhumudwa pa mau, iye ndiye munthu wangwiro, wokhoza kumanganso thupi lonse.