Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Masalimo 112:3 - Buku Lopatulika

M'nyumba mwake mudzakhala akatundu ndi chuma: Ndi chilungamo chake chikhala chikhalire.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

M'nyumba mwake mudzakhala akatundu ndi chuma: Ndi chilungamo chake chikhala chikhalire.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Banja lake lidzakhala lachuma ndi lolemera, ndipo kulungama kwake kudzakhala kwamuyaya.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Kulemera ndi chuma zili mʼnyumba yake, ndipo chilungamo chake ndi chosatha.

Onani mutuwo



Masalimo 112:3
17 Mawu Ofanana  

Ndipo udzapeza kuti pahema pako mpa mtendere; nudzazonda za m'banja mwako osasowapo kanthu.


Kumuopa Yehova ndiko chiyambi cha nzeru; onse akuchita chotero ali nacho chidziwitso chokoma; chilemekezo chake chikhalitsa kosatha.


Chochita Iye ncha ulemu, ndi ukulu: Ndi chilungamo chake chikhalitsa kosatha.


Anagawagawa, anapatsa aumphawi; chilungamo chake chikhalitsa kosatha; nyanga yake idzakwezeka ndi ulemu.


Misona ya mkango isowa nimva njala, koma iwo akufuna Yehova sadzasowa kanthu kabwino.


Idzani ananu ndimvereni ine, ndidzakulangizani zakumuopa Yehova.


M'nyumba ya wolungama muli katundu wambiri; koma m'phindu la woipa muli vuto.


Mokhala wanzeru muli katundu wofunika ndi mafuta; koma wopusa angozimeza.


Masiku ambiri ali m'dzanja lamanja lake; chuma ndi ulemu m'dzanja lake lamanzere.


Ndi ntchito ya chilungamo idzakhala mtendere; ndi zotsata chilungamo zidzakhala mtendere, ndi kukhulupirika kunthawi zonse.


Ndipo kudzakhala chilimbiko m'nthawi zako, chipulumutso chambiri, nzeru ndi kudziwa; kuopa kwa Yehova ndiko chuma chake.


Pakuti njenjete idzawadya ngati chofunda, ndi mbozi zidzawadya ngati ubweya; koma chilungamo changa chidzakhala kunthawi zonse, ndi chipulumutso changa kumibadwo yonse.


Koma muyambe mwafuna Ufumu wake ndi chilungamo chake, ndipo zonse zimenezo zidzaonjezedwa kwa inu.


monga akumva chisoni, koma akukondwera nthawi zonse; monga aumphawi, koma akulemeretsa ambiri; monga okhala opanda kanthu, ndipo akhala nazo zinthu zonse.