Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Masalimo 102:12 - Buku Lopatulika

Koma Inu, Yehova, mukhalabe kunthawi yonse; ndi chikumbukiro chanu ku mibadwomibadwo.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Koma Inu, Yehova, mukhalabe kunthawi yonse; ndi chikumbukiro chanu ku mibadwomibadwo.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Koma Inu Chauta, mumakhala pa mpando wanu waufumu mpaka muyaya. Anthu a mibadwo yonse adzakukumbukirani.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Koma Inu Yehova, muli pa mpando wanu waufumu kwamuyaya; kudziwika kwanu ndi kokhazikika ku mibado yonse.

Onani mutuwo



Masalimo 102:12
15 Mawu Ofanana  

Atuluka ngati duwa, nafota; athawa ngati mthunzi, osakhalitsa.


Pakuti ife ndife adzulo, osadziwa kanthu, popeza masiku athu a padziko lapansi ndiwo ngati mthunzi;


Ndamuka ngati mthunzi womka m'tali; ndiingidwa kwina ndi kwina ngati dzombe.


Dzina lanu, Yehova, likhala kosatha; chikumbukiro chanu, Yehova, kufikira mibadwomibadwo.


Koma Yehova akhala chikhalire, anakonzeratu mpando wachifumu wake kuti aweruze.


Mamawa uphuka bwino; madzulo ausenga, nuuma.


Ndipo Mulungu ananenanso kwa Mose, Ukatero ndi ana a Israele, Yehova Mulungu wa makolo anu, Mulungu wa Abrahamu, Mulungu wa Isaki, ndi Mulungu wa Yakobo anandituma kwa inu; ili ndi dzina langa nthawi yosatha, ichi ndi chikumbukiro changa m'mibadwomibadwo.


Atero Yehova, mfumu ya Israele ndi Mombolo wake, Yehova wa makamu, Ine ndili woyamba ndi womaliza, ndi popanda Ine palibenso Mulungu.


Ungakhale unasiyidwa ndi kudedwa, osapita munthu mwa iwe, Ine ndidzakusandutsa changwiro chosatha, chokondweretsa cha mibadwo yambiri.


Inu, Yehova, mukhala chikhalire, ndi mpando wanu wachifumu ku mibadwomibadwo.


Mulungu wamuyaya ndiye mokhaliramo mwako; ndi pansipo pali manja osatha. Ndipo aingitsa mdani pamaso pako, nati, Ononga.


Yesu Khristu ali yemweyo dzulo, ndi lero, ndi kunthawi zonse.