Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Genesis 1:24 - Buku Lopatulika

Ndipo adati Mulungu, Dziko lapansi libale zamoyo monga mwa mitundu yao, ng'ombe, ndi zokwawa, ndi zinyama za dziko lapansi monga mwa mitundu yao: ndipo kunatero.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Ndipo adati Mulungu, Dziko lapansi libale zamoyo monga mwa mitundu yao, ng'ombe, ndi zokwawa, ndi zinyama za dziko lapansi monga mwa mitundu yao: ndipo kunatero.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Ndipo Mulungu adati, “Padziko pakhale mitundu yonse ya zamoyo potsata mitundu yake: zoŵeta, zokwaŵa, ndi nyama zakuthengo, potsata mitundu yake.” Ndipo zidachitikadi.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Kenaka Mulungu anati, “Dziko lapansi litulutse zolengedwa zamoyo monga mwa mitundu yawo: ziweto, zolengedwa zokwawa ndi nyama zakuthengo, iliyonse monga mwa mtundu wake.” Ndipo zinaterodi.

Onani mutuwo



Genesis 1:24
15 Mawu Ofanana  

Ndipo panali madzulo ndipo panali m'mawa, tsiku lachisanu.


Ndipo Yehova Mulungu anaumba ndi nthaka zamoyo zonse za m'thengo, ndi mbalame zonse za m'mlengalenga; ndipo anapita nazo kwa Adamu kuti aone maina omwe adzazitcha; ndipo maina omwe onse anazitcha Adamu zamoyo zonse, omwewo ndiwo maina ao.


Za mbalame monga mwa mitundu yao, ndi zinyama monga mwa mitundu yao, ndi zokwawa zonse za dziko lapansi monga mwa mitundu yao, ziwiriziwiri monga mwa mitundu yao, zidzadza kwa iwe kuti zikhale ndi moyo.


iwo, ndi zamoyo zonse monga mwa mitundu yao, ndi zinyama zonse monga mwa mitundu yao, zokwawa zonse zokwawa padziko lapansi monga mwa mitundu yao, ndi zouluka zonse monga mwa mitundu yao, ndi mbalame zonse za mitundumitundu.


zinyama zonse, zokwawa zonse, zouluka zonse, ndi zonse zokwawa padziko lapansi, monga mwa mitundu yao, zinatuluka m'chingalawamo.


Kodi udziwa nyengo yakuswana zinkhoma? Kodi wapenyerera pakuswa mbawala?


Wampatsa kavalo mphamvu yake kodi? Wamveka pakhosi pake chenjerere chogwedezeka?


Ndani walola mbidzi ituluke yaufulu? Anaimasulira mbidzi nsinga zake ndani,


Kodi njati idzavomera kukutumikira, idzakhala ku chodyetseramo chako kodi?


Tapenya tsono mvuu ndinaipanga pamodzi ndi iwe, ikudya udzu ngati ng'ombe.


Mapiri aatali ndiwo ayenera zinkhoma; pamatanthwe mpothawirapo mbira.


Pamenepo munthu atulukira kuntchito yake, nagwiritsa kufikira madzulo.


Nyama zakuthengo ndi zoweta zonse; zokwawa, ndi mbalame zakuuluka.