Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




2 Samueli 22:18 - Buku Lopatulika

Iye anandipulumutsa kwa mdani wanga wamphamvu, kwa iwo akudana ndi ine; pakuti anandiposa mphamvu.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Iye anandipulumutsa kwa mdani wanga wamphamvu, kwa iwo akudana ndi ine; pakuti anandiposa mphamvu.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Adandipulumutsa kwa adani anga amphamvu, kwa onse amene ankadana nane; pakuti iwo anali amphamvu kwambiri kupambana ine.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Anandipulumutsa kwa mdani wanga wamphamvu, adani anga amene anali amphamvu kuposa ine.

Onani mutuwo



2 Samueli 22:18
8 Mawu Ofanana  

Ndipo Davide analankhula kwa Yehova mau a nyimbo iyi tsikuli Yehova anampulumutsa m'dzanja la adani ake onse, ndi m'dzanja la Saulo.


Iye anatumiza kuchokera kumwamba nanditenga; Iye ananditulutsa m'madzi aakulu.


Anandifikira ine tsiku la tsoka langa; koma Yehova anali mchirikizo wanga.


Ukani Yehova; ndipulumutseni, Mulungu wanga! Pakuti mwapanda adani anga onse patsaya; mwawathyola mano oipawo.


Mafupa anga onse adzanena, Yehova, afanana ndi Inu ndani, wakulanditsa wozunzika kwa iye amene amposa mphamvu, ndi wozunzika ndi waumphawi kwa iye amfunkhira?


Pamenepo adani anga adzabwerera m'mbuyo tsiku lakuitana ine. Ichi ndidziwa, kuti Mulungu avomerezana nane.


amene anatilanditsa mu imfa yaikulu yotere, nadzalanditsa; amene timyembekezera kuti adzalanditsanso;


Koma Ambuye anaima nane nandipatsa mphamvu; kuti mwa ine chilalikiro chimveke konsekonse, ndi amitundu onse amve; ndipo ndinalanditsidwa m'kamwa mwa mkango.