Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




2 Samueli 21:22 - Buku Lopatulika

Awa anai anawabala ndi Rafa ku Gati; ndipo anagwa ndi dzanja la Davide ndi la anyamata ake.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Awa anai anawabala ndi Rafa ku Gati; ndipo anagwa ndi dzanja la Davide ndi la anyamata ake.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Anthu anaiwo anali zidzukulu za Arefaimu a ku Gati, ndipo adaphedwa ndi Davide ndi ankhondo ake.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Anthu anayi amenewa anali zidzukulu za Rafa ku Gati, ndipo onse anaphedwa ndi Davide ndi ankhondo ake.

Onani mutuwo



2 Samueli 21:22
11 Mawu Ofanana  

Ndipo Isibi-Benobi, ndiye wa ana a Rafa, amene kulemera kwa mkondo wake kunali masekeli mazana atatu a mkuwa, iyeyo anavala lupanga latsopano, nati aphe Davide.


Ndipo pakutonza Israele iyeyu, Yonatani mwana a Simea mbale wa Davide anamupha.


Awa anabadwa mwa chimphonacho ku Gati, koma anagwa ndi dzanja la Davide ndi la anyamata ake.


Mwa Mulungu tidzachita molimbika mtima: Ndipo Iye adzapondereza otisautsa.


M'mahema a olungama muli liu lakufuula mokondwera Dzanja lamanja la Yehova ndi la chipulumutso:


Mwa Mulungu tidzachita molimbika mtima, ndipo Iye adzapondereza otisautsa.


Ndinabweranso ndi kuzindikira pansi pano kuti omwe athamanga msanga sapambana m'liwiro, ngakhale olimba sapambana m'nkhondo, ngakhale anzeru sapeza zakudya, ngakhale ozindikira bwino salemera, ngakhale odziwitsa sawakomera mtima; koma yense angoona zomgwera m'nthawi mwake.


Atero Yehova, wanzeru asadzitamandire m'nzeru zake, wamphamvu asadzitamandire m'mphamvu yake, wachuma asadzitamandire m'chuma chake;


Ndipo tidzatani ndi zinthu izi? Ngati Mulungu ali ndi ife, adzatikaniza ndani?


Koma m'zonsezi, ife tilakatu, mwa Iye amene anatikonda.


Ndipo tsopano, ndipatseni phiri ili limene Yehova ananenera tsiku lija; pakuti udamva tsiku lijalo kuti Aanaki anali komweko, ndi mizinda yaikulu ndi yamalinga; kapena Yehova adzakhala ndi ine, kuti ndiwaingitse monga ananena Yehova.