Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




1 Samueli 24:2 - Buku Lopatulika

Tsono Saulo anatenga anthu zikwi zitatu osankhika pakati pa Aisraele onse, namuka, kukafuna Davide ndi anthu ake m'matanthwe a zinkhoma.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Tsono Saulo anatenga anthu zikwi zitatu osankhika pakati pa Aisraele onse, namuka, kukafuna Davide ndi anthu ake m'matanthwe a zinkhoma.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Tsono adatenga ankhondo okhoza zedi 3,000 amene adaŵasankha pakati pa ankhondo onse. Adapita kukafunafuna Davide ndi anthu ake ku Matanthwe a Mbalale.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Tsono Sauli anatenga asilikali 3,000 odziwa kumenya bwino nkhondo kuchokera pakati pa Aisraeli onse ndipo anapita kukafunafuna Davide ndi anthu ake ku Matanthwe a Mbalale.

Onani mutuwo



1 Samueli 24:2
9 Mawu Ofanana  

Ndipo anati, Yehova ndiye thanthwe langa, ndi ngaka yanga, ndi Mpulumutsi wanga, wangadi.


Kodi udziwa nyengo yakuswana zinkhoma? Kodi wapenyerera pakuswa mbawala?


Mapiri aatali ndiwo ayenera zinkhoma; pamatanthwe mpothawirapo mbira.


Oweruza ao anagwetseka pambali pa thanthwe; nadzamva mau anga kuti ndiwo okondweretsa.


Woipa aunguza wolungama, nafuna kumupha.


Ndipo anditchera misampha iwo akufuna moyo wanga; ndipo iwo akuyesa kundichitira choipa alankhula zoononga, nalingirira zonyenga tsiku lonse.


Pamenepo Saulo anadzisankhira anthu zikwi zitatu a Israele; zikwi za iwowa zinali ndi Saulo ku Mikimasi, ndi kuphiri la ku Betele; ndi chikwi chimodzi anali ndi Yonatani ku Gibea wa ku Benjamini; ndipo anawauza anthu ena onse amuke ku mahema ao.


Chomwecho Saulo anabwerera polondola Davide, nakakomana ndi Afilisti; chifukwa chake anatchula dzina lake la malo aja, Thanthwe lolekanitsa.


Ndipo Saulo ananyamuka, natsikira chipululu cha Zifi, ndi anthu zikwi zitatu a Israele osankhika, kukafuna Davide m'chipululu cha Zifi.