Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




1 Samueli 18:9 - Buku Lopatulika

Ndipo kuyambira tsiku lomwelo ndi m'tsogolo mwake, Saulo anakhala maso pa Davide.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Ndipo kuyambira tsiku lomwelo ndi m'tsogolo mwake, Saulo anakhala maso pa Davide.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Motero Saulo ankamuwona ndi diso loipa Davide kuyambira tsiku limenelo.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Ndipo kuyambira tsiku limeneli Sauli ankamuchitira nsanje Davide.

Onani mutuwo



1 Samueli 18:9
11 Mawu Ofanana  

Ndipo Yakobo anaona nkhope ya Labani, taonani, siinamuonekere iye monga kale.


Kupweteka mtima nkwa nkhanza, mkwiyo usefuka; koma ndani angalakike ndi nsanje?


Ndiponso ndinapenyera mavuto onse ndi ntchito zonse zompindulira bwino, kuti chifukwa cha zimenezi anansi ake achitira munthu nsanje. Ichinso ndi chabe ndi kungosautsa mtima.


Sikuloleka kwa ine kodi kuchita chimene ndifuna ndi zanga? Kapena diso lako laipa kodi chifukwa ine ndili wabwino?


zakuba, zakupha, zachigololo, masiriro, zoipa, chinyengo, chinyanso, diso loipa, mwano, kudzikuza, kupusa:


ndiponso musampatse malo mdierekezi.


Musaipidwe wina ndi mnzake, abale, kuti mungaweruzidwe. Taonani, woweruza aima pakhomo.


Ndipo kunali m'mawa mwake, mzimu woipa wochokera kwa Mulungu unamgwira Saulo mwamphamvu, iye nalankhula moyaluka m'nyumba yake; koma Davide anaimba ndi dzanja lake, monga amachita tsiku ndi tsiku; koma m'dzanja la Saulo munali mkondo.


Koma Saulo anakwiya ndithu, ndi kunenaku kunamuipira; nati, Kwa Davide anawerengera zikwi zankhani, koma kwa ine zikwi zokha; chimperewera nchiyaninso, koma ufumu wokha?


Ndipo Saulo analankhula kwa Yonatani mwana wake, ndi anyamata ake onse kuti amuphe Davide.