Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa

Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano


Masalimo 8 - Buku Lopatulika Buku Lopatulika
Masalimo 8

Davide aimbira ulemerero wa Mulungu, ndi ulemu umene Mulungu achitira mtundu wa anthu
Kwa Mkulu wa Nyimbo: pa Gititi. Salimo la Davide.

1 Yehova, Ambuye wathu, dzina lanu liposadi nanga padziko lonse lapansi! Inu amene munaika ulemerero wanu pa thambo la kumwamba.

2 M'kamwa mwa makanda ndi oyamwa munakhazikitsa mphamvu, chifukwa cha otsutsana ndi Inu, kuti muwaletse mdani ndi wobwezera chilango.

3 Pakuona ine thambo la kumwamba lanu, ntchito ya zala zanu, mwezi ndi nyenyezi, zimene munazikhazika,

4 munthu ndani kuti mumkumbukira? Ndi mwana wa munthu kuti mucheza naye?

5 Pakuti munamchepsa pang'ono ndi Mulungu, munamveka iye korona wa ulemerero ndi ulemu.

6 Munamchititsa ufumu pa ntchito za manja anu; mudagonjetsa zonse pansi pa mapazi ake;

7 nkhosa ndi ng'ombe, zonsezo, ndi nyama zakuthengo zomwe;

8 mbalame za m'mlengalenga, ndi nsomba za m'nyanja. Zopita m'njira za m'nyanja.

9 Yehova, Ambuye wathu, dzina lanu liposadi nanga padziko lonse lapansi!

Bible Society of Malawi

Bible Society of Malawi