Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa

Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano


Masalimo 142 - Buku Lopatulika Buku Lopatulika
Masalimo 142

Pemphero pakuopsedwa kwakukulu
Chilangizo cha Davide, muja anakhala m'phanga; Pemphero.

1 Ndifuula nalo liu langa kwa Yehova; ndi mau anga ndipemba kwa Yehova.

2 Nditsanulira kudandaula kwanga pamaso pake; ndionetsa msauko wanga pamaso pake.

3 Pamene mzimu wanga unakomoka m'kati mwanga, munadziwa njira yanga. M'njira ndiyendamo ananditchera msampha.

4 Penyani kudzanja lamanja ndipo muone; palibe wondidziwa; pothawirapo pandisowa; palibe mmodzi wosamalira moyo wanga.

5 Ndinafuulira kwa inu, Yehova; ndinati, Inu ndinu pothawirapo panga, gawo langa m'dziko la amoyo.

6 Tamverani kufuula kwanga; popeza ndisauka kwambiri; ndilanditseni kwa iwo akundilondola; popeza andipambana.

7 Tulutsani moyo wanga m'ndende, kuti ndiyamike dzina lanu; olungama adzandizinga; pakuti mudzandichitira zokoma.

Bible Society of Malawi

Bible Society of Malawi