Biblia Todo Logo
Mavesi a Baibulo
- Zotsatsa -



54 Mau a Mulungu Pa Uchimo ndi Imfa

54 Mau a Mulungu Pa Uchimo ndi Imfa

Ndikufuna ndikuuzeni anzanga, tchimo lopita ku imfa ndi tchimo limene timachita modziwa bwino, mobwerezabwereza, popanda kulapa. Mulungu watiitana ife ana ake kukhala m’chiyero (1 Petro 1:16), ndipo Mulungu amatilangiza tikachimwa.

Sitikulangidwa chifukwa cha machimo athu mpaka kutaya chipulumutso chathu kapena kulekanitsidwa ndi Mulungu kosatha, koma Mulungu amatitsutsa. Pakuti Ambuye am’tsutsa iye amene am’konda, ndipo am’kwapula aliyense amene am’vomereza kukhala mwana wake (Ahebri 12:6).

Kale, tisanakhale ndi Yesu mumtima mwathu, tinali akufa chifukwa cha machimo athu ndi zolakwa zathu, koma Yesu anafa ndi kuuka kuti tikhale ndi moyo wochuluka. Chifukwa cha ichi, palibe chiweruzo cha tchimo kwa ife amene timavomeza machimo athu, kulapa, ndi kusiya machimo, chifukwa cha nsembe ya Yesu Khristu. Lero mungasangalale ndi moyo woyera, chifukwa magazi ake amatitsuka, amatikhululukira, ndi kutiyeretsa ku zoipa zonse.

Tsiku lililonse, mukadzuka, yanjanani ndi Mulungu wanu, siyani njira zanu zoipa, lapani machimo anu, ndipo mudzapeza chifundo cha Ambuye nthawi zonse. Kumbukirani kuti popanda Khristu sitingathe kuchita chilichonse, ndipo mwa Iye muli chitsimikizo chonse cha kusangalala ndi moyo waufulu.




Aroma 5:12

Chifukwa chake, monga uchimo unalowa m'dziko lapansi mwa munthu mmodzi, ndi imfa mwa uchimo; chotero imfa inafikira anthu onse, chifukwa kuti onse anachimwa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yakobo 1:15

Pamenepo chilakolakocho chitaima, chibala uchimo; ndipo uchimo, utakula msinkhu, ubala imfa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Yohane 5:16

Wina akaona mbale wake alikuchimwa tchimo losati la kuimfa, apemphere Mulungu, ndipo Iye adzampatsira moyo wa iwo akuchita machimo osati a kuimfa. Pali tchimo la kuimfa: za ililo sindinena kuti mupemphere.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 5:14

Komatu imfa inachita ufumu kuyambira kwa Adamu kufikira kwa Mose, ngakhale pa iwonso amene sanachimwe monga machimwidwe ake a Adamu, ndiye fanizo la wakudzayo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Yohane 3:14

Ife tidziwa kuti tachokera kutuluka muimfa kulowa m'moyo, chifukwa tikondana ndi abale. Iye amene sakonda akhala muimfa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 6:23

Pakuti mphotho yake ya uchimo ndi imfa; koma mphatso yaulere ya Mulungu ndiyo moyo wosatha wa mwa Khristu Yesu Ambuye wathu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 28:13

Wobisa machimo ake sadzaona mwai; koma wakuwavomereza, nawasiya adzachitidwa chifundo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Machitidwe a Atumwi 3:19

Chifukwa chake lapani, bwererani kuti afafanizidwe machimo anu, kotero kuti zidze nyengo zakutsitsimutsa zochokera kunkhope ya Ambuye;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 7:13

Ndipo tsopano chabwino chija chinandikhalira imfa kodi? Msatero ai. Koma uchimo, kuti uoneke kuti uli uchimo, wandichitira imfa mwa chabwino chija; kuti uchimo ukakhale wochimwitsa ndithu mwa lamulo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 34:21

Mphulupulu idzamupha woipa; ndipo adzawatsutsa kumlandu iwo akudana naye wolungama.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 8:8

Ndipo iwo amene ali m'thupi sangathe kukondweretsa Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yohane 8:34

Yesu anayankha iwo, nati, Indetu, indetu, ndinena kwa inu kuti yense wakuchita tchimo ali kapolo wa tchimolo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aefeso 4:26-27

Kwiyani, koma musachimwe; dzuwa lisalowe muli chikwiyire, ndiponso musampatse malo mdierekezi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Akorinto 15:56

Koma mbola ya imfa ndiyo uchimo; koma mphamvu ya uchimo ndiyo chilamulo:

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 1:32

amene ngakhale adziwa kuweruza kwake kwa Mulungu, kuti iwo amene achita zotere ayenera imfa, azichita iwo okha, ndiponso avomerezana ndi iwo akuzichita.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 7:5

Pakuti pamene tinali m'thupi, zilakolako za machimo, zimene zinali mwa chilamulo, zinalikuchita m'ziwalo zathu, kuti zibalire imfa zipatso.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 6:21

Ndipo munali nazo zobala zanji nthawi ija, m'zinthu zimene muchita nazo manyazi tsopano? Pakuti chimaliziro cha zinthu izi chili imfa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 16:25

Ilipo njira yooneka kwa mwamuna ngati yoongoka, koma matsiriziro ake ndi njira za imfa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Agalatiya 5:16

Koma ndinena, Muyendeyende ndi Mzimu, ndipo musafitse chilakolako cha thupi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 6:14

Pakuti uchimo sudzachita ufumu pa inu; popeza simuli a lamulo koma a chisomo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Levitiko 5:17

Ndipo munthu akachimwa, nakachita china cha zinthu zilizonse aziletsa Yehova; angakhale analibe kudziwa, koma wapalamula, azisenza mphulupulu yake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 2:18

Nyumba yake itsikira kuimfa, ndi mayendedwe ake kwa akufa;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Habakuku 2:5

Ndiponso vinyo ngwonyenga, ngati munthu wodzikuza, wosakhala kwao; wakukulitsa chikhumbo chake ngati kunsi kwa manda, akunga imfa, yosakhuta, koma adzisonkhanitsira amitundu onse, nadzimemezera mitundu yonse ya anthu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
2 Akorinto 5:21

Ameneyo sanadziwe uchimo anamyesera uchimo m'malo mwathu; kuti ife tikhale chilungamo cha Mulungu mwa Iye.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Genesis 2:17

koma mtengo wakudziwitsa zabwino ndi zoipa usadye umenewo; chifukwa tsiku lomwe udzadya umenewo udzafa ndithu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Genesis 3:19

m'thukuta la nkhope yako udzadya chakudya, kufikira kuti udzabwerera kunthaka: chifukwa kuti m'menemo unatengedwa: chifukwa kuti ndiwe fumbi, ndi kufumbiko udzabwerera.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Ezekieli 18:4

Taonani, miyoyo yonse ndi yanga, monga moyo wa atate momwemonso moyo wa mwana, ndiyo yanga; moyo wochimwawo ndiwo udzafa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Agalatiya 6:7-8

Musanyengedwe; Mulungu sanyozeka; pakuti chimene munthu achifesa, chimenenso adzachituta. Pakuti wakufesera kwa thupi la iye yekha, chochokera m'thupi adzatuta chivundi; koma wakufesera kwa Mzimu, chochokera mu Mzimu adzatuta moyo wosatha.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Ezekieli 18:30-32

Chifukwa chake ndidzakuweruzani inu, nyumba ya Israele, yense monga mwa njira zake, ati Ambuye Yehova. Bwererani, nimutembenukire kuleka zolakwa zanu zonse, ndipo simudzakhumudwa nazo, ndi kuonongeka nayo mphulupulu. Tayani, ndi kudzichotsera zolakwa zanu zonse zimene munalakwa nazo, ndi kudzifunira mtima watsopano, ndi mzimu watsopano; pakuti mudzaferanji inu, nyumba ya Israele? Pakuti sindikondwera nayo imfa ya wakufayo, ati Ambuye Yehova; chifukwa chake bwererani, nimukhale ndi moyo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 8:6

pakuti chisamaliro cha thupi chili imfa; koma chisamaliro cha mzimu chili moyo ndi mtendere.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Ahebri 9:27

Ndipo popeza kwaikikatu kwa anthu kufa kamodzi, ndipo atafa, chiweruziro;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 14:12

Ilipo njira yooneka kwa mwamuna ngati yoongoka; koma matsiriziro ake ndi njira za imfa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Yohane 5:16-17

Wina akaona mbale wake alikuchimwa tchimo losati la kuimfa, apemphere Mulungu, ndipo Iye adzampatsira moyo wa iwo akuchita machimo osati a kuimfa. Pali tchimo la kuimfa: za ililo sindinena kuti mupemphere. Chosalungama chilichonse chili uchimo; ndipo pali tchimo losati la kuimfa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 51:5

Onani, ndinabadwa m'mphulupulu, ndipo mai wanga anandilandira m'zoipa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 7:13

Lowani pa chipata chopapatiza; chifukwa chipata chili chachikulu, ndi njira yakumuka nayo kukuonongeka ili yotakata; ndipo ali ambiri amene alowa pa icho.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 11:19

Wolimbikira chilungamo alandira moyo; koma wolondola zoipa adzipha yekha.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Agalatiya 5:19-21

Ndipo ntchito za thupi zionekera, ndizo dama, chodetsa, kukhumba zonyansa, Taonani, ine Paulo ndinena ndi inu, kuti, ngati mulola akuduleni, Khristu simudzapindula naye kanthu. kupembedza mafano, nyanga, madano, ndeu, kaduka, zopsa mtima, zotetana, magawano, mipatuko, njiru, kuledzera, mchezo, ndi zina zotere; zimene ndikuchenjezani nazo, monga ndachita, kuti iwo akuchitachita zotere sadzalowa Ufumu wa Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 37:38

Koma olakwa adzaonongeka pamodzi; matsiriziro a oipa adzadulidwa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aefeso 2:1-3

Ndipo inu, anakupatsani moyo, pokhala munali akufa ndi zolakwa, ndi zochimwa zanu, Pakuti ife ndife chipango chake, olengedwa mwa Khristu Yesu, kuchita ntchito zabwino, zimene Mulungu anazipangiratu, kuti tikayende m'menemo. Momwemo kumbukirani, kuti kale inu amitundu m'thupi, otchedwa kusadulidwa ndi iwo otchedwa mdulidwe m'thupi, umene udachitika ndi manja; kuti nthawi ija munali opanda Khristu, alendo a padera ndi mbumba ya Israele, ndi alendo alibe kanthu ndi mapangano a malonjezano, opanda chiyembekezo, ndi opanda Mulungu m'dziko lapansi. Koma tsopano mwa Khristu Yesu inu amene munali kutali kale, anakusendezani mukhale pafupi m'mwazi wa Khristu. Pakuti Iye ndiye mtendere wathu, amene anachita kuti onse awiri akhale mmodzi, nagumula khoma lakudulitsa pakati, atachotsa udani m'thupi lake, ndiwo mau a chilamulo cha kutchulako malangizo; kuti alenge awiriwa mwa Iye yekha, akhale munthu mmodzi watsopano, ndi kuchitapo mtendere; ndi kuti akayanjanitse awiriwa ndi Mulungu, m'thupi limodzi mwa mtandawo, atapha nao udaniwo; ndipo m'mene anadza, analalikira Uthenga Wabwino wa mtendere kwa inu akutali, ndi mtendere kwa iwo apafupi; kuti mwa Iye ife tonse awiri tili nao malowedwe athu kwa Atate, mwa Mzimu mmodzi. Pamenepo ndipo simulinso alendo ndi ogonera, komatu muli a mudzi womwewo wa oyera mtima ndi a banja la Mulungu; zimene munayendamo kale, monga mwa mayendedwe a dziko lapansi lino, monga mwa mkulu wa ulamuliro wa mlengalenga, wa mzimu wakuchita tsopano mwa ana a kusamvera; omangika pa maziko a atumwi ndi aneneri, pali Khristu Yesu mwini, mwala wa pangodya; mwa Iye chimango chonse cholumikizika pamodzi bwino, chikula, chikhale Kachisi wopatulika mwa Ambuye; chimene inunso mumangidwamo pamodzi, mukhale chokhalamo Mulungu mwa Mzimu. amene ife tonsenso tinagonera pakati pao kale, m'zilakolako za thupi lathu, ndi kuchita zifuniro za thupi, ndi za maganizo, ndipo tinali ana a mkwiyo chibadwire, monganso otsalawo;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 5:22-23

Zoipa zakezake zidzagwira woipa; adzamangidwa ndi zingwe za uchimo wake. Adzafa posowa mwambo; adzasochera popusa kwambiri.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Akolose 3:6

chifukwa cha izi zomwe ukudza mkwiyo wa Mulungu pa ana a kusamvera;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yakobo 4:17

Potero kwa iye amene adziwa kuchita bwino, ndipo sachita, kwa iye kuli tchimo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Chivumbulutso 21:8

Koma amantha, ndi osakhulupirira, ndi onyansa, ndi ambanda, ndi achigololo, ndi olambira mafano, ndi onse a mabodza, cholandira chao chidzakhala m'nyanja yotentha ndi moto ndi sulufure; ndiyo imfa yachiwiri.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Petro 2:24

amene anasenza machimo athu mwini yekha m'thupi mwake pamtanda, kuti ife, titafa kumachimo, tikakhale ndi moyo kutsata chilungamo; ameneyo mikwingwirima yake munachiritsidwa nayo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 12:28

M'khwalala la chilungamo muli moyo; m'njira ya mayendedwe ake mulibe imfa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 59:2

koma zoipa zanu zakulekanitsani inu ndi Mulungu wanu; ndipo machimo anu abisa nkhope yake kwa inu, kuti Iye sakumva.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
2 Atesalonika 1:9

amene adzamva chilango, ndicho chionongeko chosatha chowasiyanitsa kunkhope ya Ambuye, ndi kuulemerero wa mphamvu yake,

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 7:13-14

Lowani pa chipata chopapatiza; chifukwa chipata chili chachikulu, ndi njira yakumuka nayo kukuonongeka ili yotakata; ndipo ali ambiri amene alowa pa icho. Pakuti chipata chili chopapatiza, ndi ichepetsa njirayo yakumuka nayo kumoyo, ndimo akuchipeza chimenecho ali owerengeka.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Akolose 3:5

Chifukwa chake fetsani ziwalozo zili padziko; dama, chidetso, chifunitso chamanyazi, chilakolako choipa, ndi chisiriro, chimene chili kupembedza mafano;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 2:6-8

amene adzabwezera munthu aliyense kolingana ndi ntchito zake; kwa iwo amene afunafuna ulemerero ndi ulemu ndi chisaonongeko, mwa kupirira pa ntchito zabwino, adzabwezera moyo wosatha; koma kwa iwo andeu, ndi osamvera choonadi, koma amvera chosalungama, adzabwezera mkwiyo ndi kuzaza,

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 10:16

Ntchito za wolungama zipatsa moyo; koma phindu la oipa lichimwitsa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 3:23

pakuti onse anachimwa, naperewera pa ulemerero wa Mulungu;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani

Pemphero kwa Mulungu

Atate wanga wachikondi ndi Baba wabwino! Ndikubwera kwa Inu kudzera mwa Ambuye wanga Yesu Khristu, ndikupemphani kuti mundithandize ndi kundimasula ku chilichonse chomwe chimandimangirira ku uchimo. Mawu anu amati: "Pakuti malipiro a uchimo ndiwo imfa, koma mphatso yaulere ya Mulungu ndiyo moyo wosatha mwa Khristu Yesu." Ambuye Yesu, limbitsani ndi kukonzanso munthu wanga wamkati, ndithandizeni kuvua munthu wakale amene ali ndi zilakolako zonyenga. Ndilitseni kuti ndisapereke malo ku uchimo m'moyo wanga, koma ndithandizeni kukana chilakolako chilichonse ndi chilichonse chomwe chimandipangitsa kuchimwa. Ambuye, simunandipatsa mzimu wa mantha, koma wa mphamvu, chikondi ndi kudziletsa. Ndithandizeni kupambana, kutseka chitseko cha uchimo ndi kuchotsa m'moyo wanga zizolowezi zoipa, chigololo, zolaula, bodza, chilakolako, umbombo, chigololo ndi chonyansa chilichonse. M'dzina la Yesu. Ameni.
Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa