Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -

Masalimo 98 - Buku Lopatulika


Alemekeze Mulungu pa chifundo ndi choonadi chao
Salimo.

1 Muimbireni Yehova nyimbo yatsopano; popeza anachita zodabwitsa: Dzanja lake lamanja, mkono wake woyera, zinamchitira chipulumutso.

2 Yehova anawadziwitsira chipulumutso chake; anaonetsera chilungamo chake pamaso pa amitundu.

3 Anakumbukira chifundo chake ndi chikhulupiriko chake kunyumba ya Israele; malekezero onse a dziko lapansi anaona chipulumutso cha Mulungu wathu.

4 Fuulirani kwa Yehova, inu, dziko lonse lapansi; kuwitsani ndi kufuulira mokondwera; inde, imbirani zomlemekeza.

5 Muimbireni Yehova zomlemekeza ndi zeze; ndi zeze ndi mau a salimo.

6 Fuulani pamaso pa Mfumu Yehova, ndi mbetete ndi liu la lipenga.

7 Nyanja ifuule ndi kudzala kwake; dziko lokhalamo anthu ndi iwo okhalamo;

8 mitsinje iombe m'manja; mapiri afuule pamodzi mokondwera.

9 Pamaso pa Yehova, popeza akudza kudzaweruza dziko lapansi; adzaweruza dziko lokhalamo anthu ndi chilungamo, ndipo mitundu ya anthu molunjika.

Bible Society of Malawi

Bible Society of Malawi
Titsatireni:



Zotsatsa