Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Yoweli 2:7 - Buku Lopatulika

Athamanga ngati amphamvu; akwera linga ngati anthu a nkhondo; niliyenda lililonse njira yake, osasokonezeka m'mabande ao.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Athamanga ngati amphamvu; akwera linga ngati anthu a nkhondo; niliyenda lililonse njira yake, osasokonezeka m'mabande ao.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Akududuka ngati ankhondo. Akukwera malinga ngati asilikali. Aliyense akuyenda pa mzere, osasempha njira yake.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Amathamanga ngati ankhondo; amakwera makoma ngati asilikali. Onse amayenda pa mizere, osaphonya njira yawo.

Onani mutuwo



Yoweli 2:7
11 Mawu Ofanana  

Saulo ndi Yonatani anali okoma ndi okondweretsa m'miyoyo yao, ndipo mu imfa yao sanasiyane; anali nalo liwiro loposa chiombankhanga, anali amphamvu koposa mikango.


Ndipo tsiku lija Davide anati, Aliyense akakantha Ayebusi, aponye m'madzi opuwala ndi akhungu amene moyo wa Davide udana nao. Chifukwa chake akuti, Akhungu ndi opuwala sangalowe m'nyumbamo.


Ndi a Asere akutuluka kukhamu, akupangira nkhondo, zikwi makumi anai.


Andipasulapasula; andithamangira ngati wamphamvu.


ndipo lili ngati mkwati wakutuluka m'chipinda mwake, likondwera ngati chiphona kuthamanga m'njira.


Dzombe lilibe mfumu, koma lituluka lonse mabwalomabwalo.


Kwerani pa makoma ake nimupasule; koma musatsirize konse; chotsani nthambi zake pakuti sizili za Yehova.


Sakankhana, ayenda lililonse m'mopita mwake; akagwa m'zida, siithyoka nkhondo yao.


Alumphira mzinda, athamanga palinga, akwerera nyumba, alowera pamazenera ngati khungu.