Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Masalimo 72:6 - Buku Lopatulika

Adzanga mvula yakugwa pa udzu wosenga, monga mvula yothirira dziko.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Adzanga mvula yakugwa pa udzu wosenga, monga mvula yothirira dziko.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Idzakhala madalitso ngati mvula yogwa pa minda ngati mvula yowaza pa nthaka!

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Iye adzakhala kugwa kwa mvula pa minda yolimidwa ngati mivumbi yothirira dziko lapansi.

Onani mutuwo



Masalimo 72:6
11 Mawu Ofanana  

Iye adzakhala ngati kuunika kwa m'mawa, potuluka dzuwa, M'mawa mopanda mitambo; pamene msipu uphuka kutuluka pansi, chifukwa cha kuwala koyera, italeka mvula.


Mukhutitsa nthaka yake yolima; mufafaniza nthumbira zake; muiolowetsa ndi mvumbi; mudalitsa mmera wake.


M'kuunika kwa nkhope ya mfumu muli moyo; kukoma mtima kwake kunga mtambo wa mvula ya masika.


Mkwiyo wa mfumu ukunga kubangula kwa mkango; koma kukoma mtima kwake kunga mame pamsipu.


ndipo ndidzaupasula; sudzadzomboleredwa kapena kulimidwa; koma padzamera lunguzi ndi minga; ndidzalamuliranso mitambo kuti isavumbwepo mvula.


Tidziwe tsono, tilondole kudziwa Yehova; kutuluka kwake kwakonzekeratu ngati matanda kucha; ndipo adzatidzera ngati mvula, ngati mvula ya masika yakuthirira dziko.


Ndipo iwo adzatha dziko la Asiriya ndi lupanga, ndi dziko la Nimirodi, ndilo polowera pake; ndipo adzatilanditsa kwa a ku Asiriya pamene alowa m'dziko lathu, pamene aponda m'kati mwa malire athu.


Chiphunzitso changa chikhale ngati mvula; maneno anga agwe ngati mame; ngati mvula yowaza pamsipu, ndi monga madontho a mvula pazitsamba.