Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Masalimo 41:9 - Buku Lopatulika

Ngakhale bwenzi langa lenileni, amene ndamkhulupirira, ndiye amene adadyako mkate wanga, anandikwezera chidendene chake.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Ngakhale bwenzi langa lenileni, amene ndamkhulupirira, ndiye amene adadyako mkate wanga, anandikwezera chidendene chake.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Ngakhalenso bwenzi langa lapamtima amene ndinkamkhulupirira, amene ankadya nane pamodzi, wandiwukira.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Ngakhale bwenzi langa la pamtima amene ndinamudalira, iye amene amadya pamodzi ndi ine watukula chidendene chake kulimbana nane.

Onani mutuwo



Masalimo 41:9
13 Mawu Ofanana  

Ndipo Abisalomu anaitana Ahitofele Mgiloni, phungu wa Davide, kumzinda wake ndiwo Gilo, pamene iye analikupereka nsembe. Ndipo chiwembucho chinali cholimba; pakuti anthu anachulukachulukabe kwa Abisalomu.


Iye anandichotsera abale anga kutali, ndi odziwana nane andiyesa mlendo konse.


mabwenzi anga enieni onse anyansidwa nane; ndi onse ndakondana nao asandulika adani anga.


Sindidzaika chinthu choipa pamaso panga; chochita iwo akupatuka padera chindiipira; sichidzandimamatira.


Pakuti ndamva kugogodera kwa ambiri, mantha pozungulira ponse. Neneza, ndipo tidzamneneza iye, ati atsamwali anga onse, amene ayang'anira kutsimphina kwanga; kapena adzakopedwa, ndipo ife tidzampambana iye, ndipo tidzambwezera chilango.


Anthu onse a akupangana nawe anakuperekeza mpaka pamalire; anthu okhala ndi mtendere nawe anakunyenga, nakuposa mphamvu; iwo akudya chakudya chako akutchera msampha pansi pako; mulibe nzeru mwa iye.


Musakhulupirira bwenzi, musatama bwenzi loyanja; usamtsegulire pakhomo pakamwa pako, ngakhale kwa iye wogona m'fukato mwako.


Ndipo Iye anayankha nati, Iye amene asunsa pamodzi ndi Ine dzanja lake m'mbale, yemweyu adzandipereka Ine.


Sindinena za inu nonse; ndidziwa amene ndawasankha: koma kuti cholemba chikwaniridwe, Iye wakudya mkate wanga anatsalimira pa Ine chidendene chake.


Koma Yesuruni anasanduka wonenepa, natazira; wasanduka wonenepa, wakula, wakuta ndi mafuta; pamenepo anasiya Mulungu amene anamlenga, napeputsa thanthwe la chipulumutso chake.