Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Masalimo 143:2 - Buku Lopatulika

Ndipo musaitane mlandu wa mtumiki wanu; pakuti pamaso panu sipadzakhala wolungama wamoyo mmodzi yense.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Ndipo musaitane mlandu wa mtumiki wanu; pakuti pamaso panu sipadzakhala wolungama wamoyo mmodzi yense.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Musandizenge mlandu ine mtumiki wanu, popeza kuti palibe munthu wamoyo amene ali wolungama pamaso panu.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Musazenge mlandu mtumiki wanu, pakuti palibe munthu wamoyo amene ndi wolungama pamaso panu.

Onani mutuwo



Masalimo 143:2
12 Mawu Ofanana  

Akachimwira Inu, popeza palibe munthu wosachimwa, ndipo mukakwiya nao ndi kuwapereka kwa adani, kuti iwo awatenge ndende kunka nao ku dziko la adani, ngati kutali kapena kufupi,


Ndipo kodi mumtsegulira maso anu wotereyo, ndi kunditenga kunena nane mlandu Inu?


Munthu nchiyani kuti akhale woyera, wobadwa ndi mkazi kuti akhale wolungama?


Potero munthu akhala bwanji wolungama kwa Mulungu? Kapena wobadwa ndi mkazi akhala woyera bwanji?


Kodi munthu adzakhala wolungama ndi kuposa Mulungu? Kodi munthu adzakhala woyera woposa Mlengi wake?


Mukasunga mphulupulu, Yehova, adzakhala chilili ndani, Ambuye?


wakusungira anthu osawerengeka chifundo, wakukhululukira mphulupulu ndi kulakwa ndi kuchimwa; koma wosamasula wopalamula; wakulanga ana ndi zidzukulu chifukwa cha mphulupulu ya atate ao, kufikira mbadwo wachitatu ndi wachinai.


Pakuti kulibe wolungama pansi pano amene achita zabwino osachimwa.


chifukwa kuti pamaso pake palibe munthu adzayesedwa wolungama ndi ntchito za lamulo; pakuti uchimo udziwika ndi lamulo.


koma podziwa kuti munthu sayesedwa wolungama pa ntchito ya lamulo, koma mwa chikhulupiriro cha Yesu Khristu, ifedi tinakhulupirira kwa Khristu Yesu, kuti tikayesedwe olungama ndi chikhulupiriro cha Khristu, ndipo si ndi ntchito za lamulo; pakuti palibe munthu adzayesedwa wolungama ndi ntchito za lamulo.


Tikanena kuti sitidachimwe, timuyesa Iye wonama, ndipo mau ake sakhala mwa ife.