Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Masalimo 139:3 - Buku Lopatulika

Muyesa popita ine ndi pogona ine, ndi njira zanga zonse muzolowerana nazo.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Muyesa popita ine ndi pogona ine, ndi njira zanga zonse muzolowerana nazo.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Mumandipenyetsetsa ndikamayenda ndiponso ndikamagona, mumadziŵa njira zanga zonse.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Mumapenyetsetsa pamene ndikutuluka ndi kugona kwanga; mumadziwa njira zanga zonse.

Onani mutuwo



Masalimo 139:3
21 Mawu Ofanana  

Ndipo pakutuluka malirowo, Davide anatumiza munthu namtenga afike kwao kunyumba yake; ndipo iyeyo anakhala mkazi wake nambalira mwana wamwamuna. Koma Yehova anaipidwa ndi chinthu chimene Davide adachita.


Ndipo anaika maboma mu Edomu; m'dziko lonse la Edomu anaika maboma, ndipo Aedomu onse anasanduka anthu a Davide. Ndipo Yehova anasunga Davide kulikonse anamukako.


Koma adziwa njira ndilowayi; atandiyesa ndidzatuluka ngati golide.


Nanga sapenya njira zanga, ndi kuwerenga moponda mwanga monse?


Ndinasamalira malangizo anu ndi mboni zanu; popeza njira zanga zonse zili pamaso panu.


Ndikaziwerenga zichuluka koposa mchenga: Ndikauka ndikhalanso nanu.


Pakuti Mulungu adzanena mlandu wa zochita zonse, ndi zobisika zonse, ngakhale zabwino ngakhale zoipa.


Tsoka kwa iwo amene afunitsa kubisira Yehova uphungu wao, ndi ntchito zao zili mumdima, ndipo amati ndani ationa ife? Ndani atidziwa ife?


Kodi munthu angathe kubisala mobisika kuti ndisamuone iye? Ati Yehova. Kodi Ine sindidzala kumwamba ndi dziko lapansi? Ati Yehova.


chouluzira chake chili m'dzanja lake, ndipo adzayeretsa padwale pake; ndipo adzasonkhanitsa tirigu wake m'nkhokwe, koma mankhusu adzatentha ndi moto wosazima.


Ndipo pokhala pamgonero, mdierekezi adatha kuika mu mtima wake wa Yudasi mwana wa Simoni Iskariote, kuti akampereke Iye,


Yesu m'mene adanena izi, anavutika mumzimu, nachita umboni, nati, Indetu, indetu, ndinena ndi inu, kuti mmodzi wa inu adzandipereka Ine.