Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Masalimo 109:3 - Buku Lopatulika

Ndipo anandizinga ndi mau a udani, nalimbana nane kopanda chifukwa.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Ndipo anandizinga ndi mau a udani, nalimbana nane kopanda chifukwa.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Ponseponse amandilankhula mau achidani, amandinena popanda chifukwa.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Andizungulira ndi mawu audani, amandinena popanda chifukwa.

Onani mutuwo



Masalimo 109:3
14 Mawu Ofanana  

Ndipo Abisalomu anaitana Ahitofele Mgiloni, phungu wa Davide, kumzinda wake ndiwo Gilo, pamene iye analikupereka nsembe. Ndipo chiwembucho chinali cholimba; pakuti anthu anachulukachulukabe kwa Abisalomu.


Tsopano anatizinga m'mayendedwe athu, apenyetsetsa m'maso kuti atigwetse pansi.


Ng'ombe zamphongo zambiri zandizinga; mphongo zolimba za ku Basani zandizungulira.


Adani anga asandikondwerere ine monyenga; okwiya nane kopanda chifukwa asanditsinzinire.


Pakuti salankhula zamtendere, koma apangira chiwembu odekha m'dziko.


Pakuti ananditchera ukonde wao m'mbunamo kopanda chifukwa, anakumbira moyo wanga dzenje kopanda chifukwa.


Ondida kopanda chifukwa achuluka koposa tsitsi la pamutu panga; ofuna kunditha, ndiwo adani anga monama, ali ndi mphamvu. Pamenepo andibwezetsa chosafunkha ine.


Zinandizungulira ngati madzi tsiku lonse; zinandizinga pamodzi.


Efuremu andizinga ndi bodza, ndi nyumba ya Israele ndi chinyengo, ndi Yuda apikisana ndi Mulungu, ndiye Woyera wokhulupirika.


Nati iye, Chifukwa ninji mbuye wanga amalondola mnyamata wake? Pakuti ndachitanji? Kapena m'dzanja langa muli choipa chotani?