Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Masalimo 10:1 - Buku Lopatulika

Muimiranji patali, Yehova? Mubisaliranji m'nyengo za nsautso?

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Muimiranji patali, Yehova? Mubisaliranji m'nyengo za nsautso?

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Chifukwa chiyani mumaima kutali nafe, Inu Chauta? Chifukwa chiyani mumabisala pamene tili pa mavuto?

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Nʼchifukwa chiyani Yehova mwayima patali? Chifukwa chiyani mukudzibisa nokha pa nthawi ya mavuto?

Onani mutuwo



Masalimo 10:1
13 Mawu Ofanana  

Mubisiranji nkhope yanu, ndi kundiyesa mdani wanu?


akachita Iye kulamanzere, sindimpenyerera; akabisala kulamanja, sindimuona.


Iye akapatsa mpumulo adzamtsutsa ndani? Akabisa nkhope yake adzampenyerera ndani? Chikachitika pa mtundu wa anthu, kapena pa munthu, nchimodzimodzi;


Mulungu wanga, Mulungu wanga, mwandisiyiranji ine? Mukhaliranji kutali kwa chipulumutso changa, ndi kwa mau a kubuula kwanga?


Musandibisire ine nkhope yanu; musachotse kapolo wanu ndi kukwiya. Inu munakhala thandizo langa; musanditaye, ndipo musandisiye Mulungu wa chipulumutso changa.


Inu, Yehova, munakhazikitsa phiri langa ndi kuyanja kwanu; munabisa nkhope yanu; ndinaopa.


Mubisiranji nkhope yanu, ndi kuiwala kuzunzika ndi kupsinjika kwathu?


Pakuti moyo wathu waweramira kufumbi, pamimba pathu pakangamira dziko lapansi.


Mulungu ndiye pothawirapo pathu ndi mphamvu yathu, thandizo lopezekeratu m'masautso.


Yehova mutayiranji moyo wanga? Ndi kundibisira nkhope yanu?


Inu, chiyembekezo cha Israele, Mpulumutsi wake nthawi ya msauko, bwanji mukhala ngati mlendo m'dziko, ngati woyendayenda amene apatuka usiku?


Bwanji mukhala ngati munthu wodabwa, ngati munthu wamphamvu wosatha kupulumutsa? Koma Inu, Yehova, muli pakati pathu, titchedwa ndi dzina lanu; musatisiye.