Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Genesis 1:30 - Buku Lopatulika

ndiponso ndapatsa zinyama zonse za dziko lapansi, ndi mbalame zonse za m'mlengalenga, ndi zokwawa zonse za dziko lapansi m'mene muli moyo, therere laliwisi lonse likhale chakudya: ndipo kunatero.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

ndiponso ndapatsa zinyama zonse za dziko lapansi, ndi mbalame zonse za m'mlengalenga, ndi zakukwawa zonse za dziko lapansi m'mene muli moyo, therere laliwisi lonse likhale chakudya: ndipo kunatero.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Koma nyama zonse zakuthengo, mbalame, ndi zokwaŵa zonse, ndazipatsa msipu kuti zizidya,” ndipo zidachitikadi momwemo.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Ndaperekanso msipu kwa nyama zonse za pa dziko lapansi ndi kwa mbalame zamlengalenga ndi kwa cholengedwa chamoyo chilichonse chimene chimakwawa, chilichonse chimene chili ndi moyo.” Ndipo zinachitikadi.

Onani mutuwo



Genesis 1:30
11 Mawu Ofanana  

Ndipo iwe udzitengereko wekha zakudya zonse zodyedwa, nudzisonkhanitsire izi wekha: ndipo zidzakhala zakudya za iwe ndi za iwo.


Zoyenda zonse zamoyo zidzakhala zakudya zanu; monga therere laliwisi ndakupatsani inu zonsezo.


Ana ake akumwa mwazi, ndipo pomwe pali ophedwa, apo pali icho.


Ana ao akhala ojincha, akulira kuthengo, achoka osabwerera kwa amao.


Poyenda ponse pamapiri mpa busa pake; ilondola chachiwisi chilichonse.


Tapenya tsono mvuu ndinaipanga pamodzi ndi iwe, ikudya udzu ngati ng'ombe.


Pakuti mapiri aiphukitsira chakudya, kumene zisewera nyama zonse zakuthengo.


Ameretsa msipu ziudye ng'ombe, ndi zitsamba achite nazo munthu; natulutse chakudya chochokera m'nthaka;


Amene apatsa zoweta chakudya chao, ana a khwangwala alikulira.