Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Eksodo 22:14 - Buku Lopatulika

Munthu akabwereka chinthu kwa mnansi wake, ndipo chiphwetekwa, kapena chifa, mwiniyo palibe, azilipa ndithu.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Munthu akabwereka chinthu kwa mnansi wake, ndipo chiphwetekwa, kapena chifa, mwiniyo palibe, azilipa ndithu.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

“Munthu akabwereka choŵeta kwa mnzake, tsono choŵeta chija nkupweteka mpaka kufa pamene sichili kwa mwiniwakeyo, wobwerekayo alipire ndithu choŵetacho.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

“Ngati munthu abwereka chiweto cha mnzake ndipo chiweto chija nʼkuvulala kapena kufa chikanali ndi iyebe, wobwerekayo ayenera kulipira.

Onani mutuwo



Eksodo 22:14
11 Mawu Ofanana  

Panali enanso akuti, Takongola ndalama za msonkho wa mfumu; taperekapo chikole minda yathu, ndi minda yathu yampesa.


Woipa akongola, wosabweza, koma wolungama achitira chifundo, napereka.


mwini dzenje azilipa; azilipa ndalama kwa mwini nyamayo, koma yakufayo ndi yake.


lumbiro la Yehova likhale pakati pa iwo awiri, kuti sanatulutse dzanja lake pa chuma cha mnansi wake; ndipo mwiniyo azivomereza, ndipo asalipe.


Ngati chajiwa ndithu, abwere nacho chikhale mboni; asalipe pa chojiwacho.


Akakhalapo mwiniyo, asalipe; ngati chagwirira ntchito yakulipira, chadzera kulipira kwake.


Munthu akakantha nyama kuti ife, ambwezere ina; moyo kulipa moyo.


Kwa iye wopempha iwe umpatse, ndipo kwa iye wofuna kukukongola usampotolokere.


Koma takondanani nao adani anu, ndi kuwachitira zabwino, ndipo kongoletsani osayembekeza kanthu konse, ndipo mphotho yanu idzakhala yaikulu, ndipo inu mudzakhala ana a Wamkulukuluyo; chifukwa Iye achitira zokoma anthu osayamika ndi oipa.


Chilekererocho ndichi: okongoletsa onse alekerere chokongoletsa mnansi wake; asachifunse kwa mnansi wake, kapena mbale wake; popeza analalikira chilekerero cha Yehova.