Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Eksodo 12:30 - Buku Lopatulika

Ndipo Farao anauka usiku, iye ndi anyamata ake onse ndi Aejipito onse; ndipo kunali kulira kwakukulu mu Ejipito; pakuti panalibe nyumba yopanda wakufa m'mwemo.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Ndipo Farao anauka usiku, iye ndi anyamata ake onse ndi Aejipito onse; ndipo kunali kulira kwakukulu m'Ejipito; pakuti panalibe nyumba yopanda wakufa m'mwemo.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Farao ndi nduna zake zonse, pamodzi ndi Aejipito onse, adadzuka pakati pa usiku, ndipo m'dziko lonse la Ejipito munali maliro okhaokha, chifukwa panalibe banja lopanda mwana wakufa.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Farao ndi nduna zake zonse ndiponso Aigupto onse anadzuka pakati pa usiku, ndipo kunali kulira kwakukulu mʼdziko lonse la Igupto, pakuti panalibe nyumba imene munalibe munthu wakufa.

Onani mutuwo



Eksodo 12:30
9 Mawu Ofanana  

Analambulira mkwiyo wake njira; sanalekerere moyo wao usafe, koma anapereka moyo wao kumliri.


Ndipo ananena nao, Momwemo, Yehova akhale nanu ngati ndilola inu ndi ana aang'ono anu mumuke; chenjerani pakuti pali choipa pamaso panu.


Ndipo kudzakhala kulira kwakukulu m'dziko lonse la Ejipito, kunalibe kunzake kotere, sikudzakhalanso kunzake kotere.


Wotseka makutu ake polira waumphawi, nayenso adzalira koma osamvedwa.


Ndi m'minda yonse yamipesa mudzakhala kulira, pakuti ndipita pakati pako, ati Yehova.


Patsogolo pake panapita mliri, ndi makala amoto anatuluka pa mapazi ake.


Koma pakati pa usiku panali kufuula, Onani, mkwati! Tulukani kukakomana naye.


Pakuti chiweruziro chilibe chifundo kwa iye amene sanachite chifundo; chifundo chidzitamandira kutsutsana nacho chiweruziro.


Ndipo amene anapanda kufa anagwidwa ndi mafundowo; ndi kulira kwa mzindawo kunakwera kumwamba.