Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




2 Samueli 8:14 - Buku Lopatulika

Ndipo anaika maboma mu Edomu; m'dziko lonse la Edomu anaika maboma, ndipo Aedomu onse anasanduka anthu a Davide. Ndipo Yehova anasunga Davide kulikonse anamukako.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Ndipo anaika maboma m'Edomu; m'dziko lonse la Edomu anaika maboma, ndipo Aedomu onse anasanduka anthu a Davide. Ndipo Yehova anasunga Davide kulikonse anamukako.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Tsono adaika zigono za ankhondo pena ndi pena m'dziko la Edomu. Mu Edomu monse munali timagulu ta ankhondo, choncho Aedomu onse adasanduka otumikira Davide. Motero Chauta adampambanitsa Davide kulikonse kumene ankapita.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Iye anayika maboma mʼdera lonse la Edomu, ndipo Aedomu onse anakhala pansi pa Davide. Yehova ankapambanitsa Davide kulikonse kumene ankapita.

Onani mutuwo



2 Samueli 8:14
18 Mawu Ofanana  

Yehova ndipo anati kwa iye, Mitundu iwiri ili m'mimba mwako, magulu awiri a anthu adzatuluka m'mimba mwako; gulu lina lidzapambana mphamvu ndi linzake; wamkulu adzakhala kapolo wa wamng'ono.


Anthu akutumikire iwe, mitundu ikuweramire iwe; uchite ufumu pa abale ako, ana a amai ako akuweramire iwe. Wotemberereka aliyense akutemberera iwe, wodalitsika aliyense akudalitsa iwe.


Ndipo Davide anakula chikulire chifukwa Yehova Mulungu wa makamu anali naye.


Ndipo ndinali nawe kulikonse unamukako, ndi kuononga adani ako onse pamaso pako; ndipo ndidzamveketsa dzina lako, monga dzina la akulu ali padziko lapansi.


Ndipo Davide anakhala mfumu ya Aisraele onse, Davide naweruza ndi chilungamo milandu ya anthu onse.


Pamenepo Davide anaika maboma mu Aramu wa Damasiko. Ndipo Aaramu anasanduka anthu a Davide, nabwera nayo mitulo. Ndipo Yehova anamsunga Davide kulikonse anamukako.


Pakuti pamene Davide adali mu Edomu, ndipo Yowabu kazembe wa nkhondo adanka kukaika akufawo, atapha amuna onse mu Edomu;


Ndipo mu Edomu munalibe mfumu, koma kazembe wa mfumu.


Yehosafati anamanga zombo za ku Tarisisi kukatenga golide ku Ofiri; koma sizinamuke, popeza zinaphwanyika pa Eziyoni-Gebere.


Anapha Aedomu mu Chigwa cha Mchere zikwi khumi, nalanda Sela ndi nkhondo, nautcha dzina lake Yokotele mpaka lero lino.


Ndipo Yehova anali naye, nachita iye mwanzeru kulikonse anamukako, napandukira mfumu ya Asiriya osamtumikira.


Ndipo anaika asilikali a boma mu Edomu; ndi Aedomu onse anasanduka anthu a Davide. Ndipo Yehova anasunga Davide kulikonse anamukako.


Mwatitaya Mulungu, mwatipasula; mwakwiya; tibwezereni.