Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




2 Samueli 23:14 - Buku Lopatulika

Pamenepo Davide anali m'linga, ndi boma la Afilisti linali mu Betelehemu.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Pamenepo Davide anali m'linga, ndi boma la Afilisti linali m'Betelehemu.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Pamenepo nkuti Davide ali m'phanga muja, ndipo kagulu kankhondo ka Afilisti kali ku Betelehemu.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Nthawi imeneyo Davide anali mu linga, ndipo boma la Afilisti linali ku Betelehemu.

Onani mutuwo



2 Samueli 23:14
11 Mawu Ofanana  

Ndipo anafa Rakele, naikidwa panjira ya ku Efurata (ndiwo Betelehemu).


Koma pamene Afilisti anamva kuti adamdzoza Davide mfumu ya Israele, Afilisti onse anakwera kukafuna Davide; ndipo Davide anachimva natsikira kungaka kuja.


Ndipo anadza ena a ana a Benjamini ndi Yuda kulinga kwa Davide.


Ndipo m'tsogolo mwake mudzafika kuphiri la Mulungu, kumene kuli kaboma ka Afilisti; ndipo kudzali kuti pakufika inu kumzindako mudzakomana ndi gulu la aneneri, alikutsika kumsanje ndi chisakasa, ndi lingaka, ndi chitoliro, ndi zeze, pamaso pao; iwo adzanenera;


Ndipo a ku kaboma ka Afilisti anatuluka kunja ku mpata wa ku Mikimasi.


Ndipo Aisraele onse anamva kunena kuti Saulo anathyola kaboma ka Afilisti, ndi kuti Afilisti anyansidwa ndi Aisraele. Ndipo anthuwo anasonkhana kwa Saulo ku Giligala.


Ndipo Yonatani ananena ndi mnyamata wonyamula zida zake, Tiye tipite ku kaboma ka osadulidwa awa; kapena Yehova adzatigwirira ntchito; pakuti palibe chomletsa Yehova kupulumutsa angakhale ndi ambiri kapena ndi owerengeka.


Motero Davide anachoka kumeneko, napulumukira ku phanga la ku Adulamu; ndipo pamene abale ake ndi banja lonse la atate wake anamva, iwo anatsikira kumeneko kwa iye.


Ndipo Davide analumbirira Saulo. Saulo namuka kwao; koma Davide ndi anthu ake anakwera kunka kungaka.