Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa

Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano


Masalimo 15 - Buku Lopatulika Buku Lopatulika
Masalimo 15

Chikhalidwe cha munthu woona wa Mulungu
Salimo la Davide.

1 Yehova, ndani adzagonera m'chihema mwanu? Adzagonera ndani m'phiri lanu lopatulika?

2 Iye wakuyendayo mokwanira, nachita chilungamo, nanena zoonadi mumtima mwake.

3 Amene sasinjirira ndi lilime lake, nachitira mnzake choipa, ndipo satola miseche pa mnansi wake.

4 M'maso mwake munthu woonongeka anyozeka; koma awachitira ulemu akuopa Yehova. Atalumbira kwa tsoka lake, sasintha ai.

5 Ndalama zake sakongoletsa mofuna phindu lalikulu, ndipo salandira chokometsera mlandu kutsutsa wosachimwa. Munthu wakuchita izi sadzagwedezeka kunthawi zonse.

Bible Society of Malawi

Bible Society of Malawi