Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa

Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano


Masalimo 110 - Buku Lopatulika Buku Lopatulika
Masalimo 110

Ufumu wa Ambuye
Salimo la Davide.

1 Yehova ananena kwa Ambuye wanga, Khalani padzanja lamanja langa, kufikira nditaika adani anu chopondapo mapazi anu.

2 Yehova adzatumiza ndodo ya mphamvu yanu kuchokera ku Ziyoni; chitani ufumu pakati pa adani anu.

3 Anthu anu adzadzipereka eni ake tsiku la chamuna chanu: M'moyera mokometsetsa, mobadwira matanda kucha, muli nao mame a ubwana wanu.

4 Yehova walumbira, ndipo sadzasintha, Inu ndinu wansembe kosatha monga mwa chilongosoko cha Melkizedeki.

5 Ambuye padzanja lamanja lako adzaphwanya mafumu tsiku la mkwiyo wake.

6 Adzaweruza mwa amitundu, adzadzaza dziko ndi mitembo; adzaphwanya mitu m'maiko ambiri.

7 Adzamwa kumtsinje wa panjira; chifukwa chake adzaweramutsa mutu wake.

Bible Society of Malawi

Bible Society of Malawi