Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa

Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano


Masalimo 11 - Buku Lopatulika Buku Lopatulika
Masalimo 11

Yehova asunga anthu ake nalanga oipa
Kwa Mkulu wa Nyimbo. Salimo la Davide.

1 Ndakhulupirira Yehova, mutani nkunena kwa moyo wanga, Thawirani kuphiri lanu ngati mbalame?

2 Pakuti, onani, oipa akoka uta, apiringidza muvi wao pansinga, kuwaponyera mumdima oongoka mtima.

3 Akapasuka maziko, wolungama angachitenji?

4 Yehova ali mu Kachisi wake woyera, Yehova, mpando wachifumu wake uli mu Mwamba; apenyerera ndi maso ake, ayesa ana a anthu ndi zikope zake.

5 Yehova ayesa wolungama mtima, koma moyo wake umuda woipa ndi iye wakukonda chiwawa.

6 Adzagwetsa pwatapwata misampha pa oipa; moto ndi miyala ya sulufure, ndi mphepo yoopsa zidzawagawikira m'chikho chao.

7 Pakuti Yehova ndiye wolungama; akonda zolungama; woongoka mtima adzapenya nkhope yake.

Bible Society of Malawi

Bible Society of Malawi