Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Yohane 3:9 - Buku Lopatulika

Nikodemo anayankha nati kwa Iye, Izi zingatheke bwanji?

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Nikodemo anayankha nati kwa Iye, Izi zingatheke bwanji?

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Nikodemo adafunsa kuti, “Zimenezi zingachitike bwanji?”

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Nekodimo anafunsa kuti, “Kodi izi zingatheke bwanji?”

Onani mutuwo



Yohane 3:9
9 Mawu Ofanana  

Koma mayendedwe a olungama akunga kuunika kwa mbandakucha, kunkabe kuwala kufikira usana woti mbee.


Ndipo ndidzayendetsa akhungu m'khwalala, limene iwo salidziwa, m'njira zimene iwo sazidziwa ndidzawatsogolera; ndidzawalitsa mdima m'tsogolo mwao, ndi kulungamitsa malo okhota. Zinthu izi Ine ndidzachita, ndipo sindidzawasiya.


Koma Maria anati kwa mngelo, Ichi chidzachitika bwanji, popeza ine sindidziwa mwamuna?


Yesu anayankha nati kwa iye, Kodi uli mphunzitsi wa Israele, ndipo sudziwa izi?


Nikodemo ananena kwa Iye, Munthu akhoza bwanji kubadwa atakalamba? Kodi akhoza kulowanso m'mimba ya amake ndi kubadwa?


Mphepo iomba pomwe ifuna, ndipo ukumva mau ake, koma sudziwa kumene ichokera, ndi kumene imuka; chotero aliyense wobadwa mwa Mzimu.


Pamenepo Ayuda anatetana wina ndi mnzake ndi kunena, Akhoza bwanji ameneyu kutipatsa ife kudya thupi lake?


Pamenepo ambiri a ophunzira ake, pakumva izi, anati, Mau awa ndi osautsa; akhoza kumva awa ndani?