Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Numeri 32:16 - Buku Lopatulika

Ndipo anayandikiza, nati Tidzamangira zoweta zathu makola kuno, ndi ana athu mizinda;

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Ndipo anayandikiza, nati Tidzamangira zoweta zathu makola kuno, ndi ana athu midzi;

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Tsono iwo adasendera kwa Mose namuuza kuti, “Poyamba mutilole kuti timange kuno makola a nkhosa zathu, ndi mizinda yoti ana athu azikhalamo.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Ndipo iwo anabwera kwa Mose namuwuza kuti, “Ife tikufuna kumanga makola a ziweto zathu kuno ndi mizinda yokhalamo akazi athu ndi ana athu.

Onani mutuwo



Numeri 32:16
7 Mawu Ofanana  

Ndipo Yakobo anankabe ulendo wake ku Sukoti, namanga nyumba yake pamenepo, namanga makola a zoweta zake: chifukwa chake dzina lake la kumeneko ndi Sukoti.


Isakara ndiye bulu wolimba, alinkugona pakati pa makola.


Pakuti mukabwerera m'mbuyo kusamtsata Iye, adzawasiyanso m'chipululu, ndipo mudzaononga anthu awa onse.


koma ife tidzakhala okonzeka ndi kufulumira pamaso pa ana a Israele, kufikira tidawafikitsa kumalo kwao; ndi ang'ono athu adzakhala mizinda ya malinga chifukwa cha okhala m'dzikomo.


Wa fuko la ana a Dani, kalonga Buki mwana wa Yogili.


Koma akazi anu, ndi ana anu, ndi zoweta zanu, (ndidziwa muli nazo zoweta zambiri), zikhale m'mizinda yanu imene ndinakupatsani;


Ndipo anadzisankhira gawo loyamba, popeza kumeneko kudasungika gawo la wolamulira; ndipo anadza ndi mafumu a anthu, anachita chilungamo cha Yehova, ndi maweruzo ake ndi Israele.