Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Numeri 15:27 - Buku Lopatulika

Ndipo akachimwa munthu mmodzi osati dala, abwere nayo mbuzi yaikazi ya chaka chimodzi, ikhale nsembe yauchimo.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Ndipo akachimwa munthu mmodzi osati dala, abwere nayo mbuzi yamsoti ya chaka chimodzi, ikhale nsembe yauchimo.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

“Ngati munthu mmodzi alakwa mosadziŵa, apereke mbuzi yaikazi ya chaka chimodzi kuti ikhale nsembe yopepesera machimo.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

“ ‘Koma ngati munthu mmodzi achimwa mosadziwa, ayenera kubweretsa mbuzi yayikazi ya chaka chimodzi kuti ikhale nsembe yopepesera machimo.

Onani mutuwo



Numeri 15:27
7 Mawu Ofanana  

Lankhula ndi ana a Israele, ndi kuti, Munthu akachimwa, osati dala, pa china cha zinthu zilizonse aziletsa Yehova, nakachitapo kanthu;


pamenepo abwere nacho chopereka chake kwa Yehova, nkhosa yamphongo ya chaka chimodzi yopanda chilema, ikhale nsembe yopsereza, ndi nkhosa yaikazi yopanda chilema ikhale nsembe yauchimo, ndi nkhosa yamphongo yopanda chilema ikhale nsembe yoyamika;


Koma iye amene sanachidziwe, ndipo anazichita zoyenera mikwapulo, adzakwapulidwa pang'ono. Ndipo kwa munthu aliyense adampatsa zambiri, kwa iye adzafuna zambiri; ndipo amene anamuikizira zambiri, adzamuuza abwezere zoposa.


Nthawi za kusadziwako tsono Mulungu analekerera; koma tsopanotu alinkulamulira anthu onse ponseponse atembenuke mtima;


Ndipo tsopano, abale, ndidziwa kuti munachichita mosadziwa, monganso akulu anu.


ndingakhale kale ndinali wamwano, ndi wolondalonda, ndi wachipongwe; komatu anandichitira chifundo, popeza ndinazichita wosazindikira, wosakhulupirira;