Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Mateyu 9:1 - Buku Lopatulika

Ndipo Iye analowa m'ngalawa, naoloka, nadza kumzinda kwao.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Ndipo Iye analowa m'ngalawa, naoloka, nadza kumudzi kwao.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Yesu adaloŵa m'chombo naoloka nyanja, nkukafika ku mzinda wakwao.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesu analowa mʼbwato nawoloka, ndipo anabwera ku mudzi wa kwawo.

Onani mutuwo



Mateyu 9:1
8 Mawu Ofanana  

ndipo anachoka ku Nazarete nadza nakhalitsa Iye mu Kapernao wa pambali pa nyanja, m'malire a Zebuloni ndi Nafutali:


Musamapatsa chopatulikacho kwa agalu, ndipo musamaponya ngale zanu patsogolo pa nkhumba, kuti zingazipondereze ndi mapazi ao, ndi potembenuka zingang'ambe inu.


Ndipo Yesu, poona makamu ambiri a anthu akumzungulira Iye, analamulira ophunzira amuke kutsidya lina.


Ndipo pamene Iye atalowa m'ngalawa, ophunzira ake anamtsata Iye.


Ndipo pamene Yesu anaolokanso mungalawa tsidya lina, khamu lalikulu linasonkhana kwa Iye; ndipo Iye anali pambali pa nyanja.


Ndipo anthu aunyinji onse a dziko la Agerasa loyandikira anamfunsa Iye achoke kwa iwo; chifukwa anagwidwa ndi mantha aakulu. Ndipo Iye analowa m'ngalawa, nabwerera.


Ndipo pakubwera Yesu, khamu la anthu linamlandira Iye; pakuti onse analikumlindira Iye.


Iye wakukhala wosalungama achitebe zosalungama; ndi munthu wonyansa akhalebe wonyansa; ndi iye wakukhala wolungama achitebe cholungama; ndi iye amene ali woyera akhalebe woyeretsedwa.