Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Masalimo 17:9 - Buku Lopatulika

kundilanditsa kwa oipa amene andipasula, adani a pa moyo wanga amene andizinga.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

kundilanditsa kwa oipa amene andipasula, adani a pa moyo wanga amene andizinga.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

kuti asandiwone anthu oipa ofuna kupasula, ndiye kuti adani anga oopsaŵa amene akundizinga.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

kuchoka kwa oyipa amene amandizinga ine, kuchoka kwa anthu amene ndi adani anga, amene andizungulira ine.

Onani mutuwo



Masalimo 17:9
8 Mawu Ofanana  

Ndipo ndaikira anthu anga Israele malo, ndi kuwaoka, kuti akhale m'malo mwao osasunthikanso; ndi ana osalungama sadzawapululanso monga poyamba paja;


Pobisalira pamaso panu mudzawabisa kwa chiwembu cha munthu, mudzawabisa iwo mumsasa kuti muwalanditse pa kutetana kwa malilime.


Andibwezera choipa m'malo mwa chokoma, inde, asaukitsa moyo wanga.


Athe nzeru nachite manyazi iwo akufuna moyo wanga; abwezedwe m'mbuyo nasokonezeke iwo akundipangira chiwembu.


Pakuti ananditchera ukonde wao m'mbunamo kopanda chifukwa, anakumbira moyo wanga dzenje kopanda chifukwa.


mdani alondole moyo wanga, naupeze; naupondereze pansi moyo wanga, naukhalitse ulemu wanga m'fumbi.


Ndipo Saulo anamuka mbali ina ya phiri, Davide ndi anthu ake kuseri kwake; ndipo Davide anafulumira kuthawa, chifukwa cha kuopa Saulo; popeza Saulo ndi anthu ake anazinga Davide ndi anthu ake kwete kuti awagwire.


Ndiponso atate wanga, penyani, inde penyani mkawo wa mwinjiro wanu m'dzanja langa; popeza ndinadula mkawo wa mwinjiro wanu, osakuphani, mudziwe, nimuone kuti mulibe choipa kapena kulakwa m'dzanja langa, ndipo sindinakuchimwirani, chinkana inu musaka moyo wanga kuti muugwire.