Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Masalimo 1:4 - Buku Lopatulika

Oipa satero ai; koma akunga mungu wouluka ndi mphepo.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Oipa satero ai; koma akunga mungu wouluka ndi mphepo.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Anthu oipa sali choncho, ali ngati mungu wouluzika ndi mphepo.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Sizitero ndi anthu oyipa! Iwo ali ngati mungu umene umawuluzidwa ndi mphepo.

Onani mutuwo



Masalimo 1:4
9 Mawu Ofanana  

Ngati akunga ziputu zomka ndi mphepo, ngati mungu wouluzika ndi nkuntho?


Momwemo mayendedwe a onse oiwala Mulungu; ndi chiyembekezo cha onyoza Mulungu; chidzatayika.


Akhale monga mungu kumphepo, ndipo mngelo wa Yehova awapirikitse.


Koma anapita ndipo taona, kwati zii; ndipo ndinampwaira osampeza.


Mitundu ya anthu idzathamanga ngati kuthamanga kwa madzi ambirimbiri; koma Iye adzawadzudzula, ndipo iwo adzathawira patali, nadzapirikitsidwa monga mankhusu a pamapiri patsogolo pa mphepo, ndi monga fumbi lokwetera patsogolo pa mkuntho wa mphepo.


Koma khamu la achilendo ako lidzafanana ndi fumbi losalala, ndi khamu la oopsa lidzakhala monga mungu wochokachoka; inde kudzaoneka modzidzimuka dzidzidzi.


Chifukwa chake ndidzabalalitsa iwo, monga ziputu zakupita, ndi mphepo ya kuchipululu.


Chifukwa chake adzakhala ngati mtambo wa m'mawa, ndi ngati mame akamuka mamawa, ngati mungu umene mphepo iuuluza kudwale, ndi ngati utsi wotuluka kukafwambira.


chouluzira chake chili m'dzanja lake, ndipo adzayeretsa padwale pake; ndipo adzasonkhanitsa tirigu wake m'nkhokwe, koma mankhusu adzatentha ndi moto wosazima.