Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti

- Zotsatsa -




Masalimo 1:4 - Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

4 Sizitero ndi anthu oyipa! Iwo ali ngati mungu umene umawuluzidwa ndi mphepo.

Onani mutuwo Koperani

Buku Lopatulika

4 Oipa satero ai; koma akunga mungu wouluka ndi mphepo.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

4 Oipa satero ai; koma akunga mungu wouluka ndi mphepo.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

4 Anthu oipa sali choncho, ali ngati mungu wouluzika ndi mphepo.

Onani mutuwo Koperani




Masalimo 1:4
9 Mawu Ofanana  

Nʼkangati kamene iwo amakhala ngati phesi lowuluka ndi mphepo, ngati mungu wowuluzika ndi kamvuluvulu?


Ndimo mmene amachitira anthu onse amene amayiwala Mulungu; ndi mmene chiyembekezo cha munthu wosapembedza Mulungu chimathera.


Akhale ngati mankhusu owuluka ndi mphepo pamene mngelo wa Yehova akuwapirikitsa.


Koma sanachedwe kumwalira ndipo sanaonekenso; ngakhale ndinamuyangʼanayangʼana, sanapezekenso.


Ngakhale ankhondo a mitundu ina akubwera ndi mkokomo ngati wa madzi ambiri, koma adzathawira kutali Mulungu akadzawadzudzula. Yehova adzawapirikitsa ngati mankhusu owuluka ndi mphepo pa phiri, ndi ngati fumbi la kamvuluvulu asanayambe.


Koma chigulu cha adani ako chidzasanduka chifwirimbwiti. Chigulu cha ankhondo achilendo chidzabalalika ngati mungu wowuluzika ndi mphepo. Mwadzidzidzi ndi mosayembekezereka,


“Ine ndidzakumwazani ngati mankhusu amene amawuluka ndi mphepo ya ku chipululu.


Choncho adzakhala ngati nkhungu yammawa, ngati mame amene amakamuka msanga, ngati mungu wowuluka kuchokera pa malo opunthira tirigu, ngati utsi umene ukutulukira pa zenera.


Mʼdzanja lake muli chopetera ndipo adzayeretsa popunthirapo pake nadzathira tirigu wake mʼnkhokwe ndi kutentha zotsalira zonse ndi moto wosazima.”


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa