Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Eksodo 9:2 - Buku Lopatulika

Pakuti ukakana kuwalola amuke, ndi kuwagwira chigwiritsire,

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Pakuti ukakana kuwalola amuke, ndi kuwagwira chigwiritsire,

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Koma ukakananso kuŵalola kuti apite, ndi kuŵaletsa ndithu,

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Koma ngati ukana kuti apite ndi kupitiriza kuwaletsa,

Onani mutuwo



Eksodo 9:2
15 Mawu Ofanana  

Indedi Mulungu adzaphwanya mutu wa adani ake, pakati pamutu pa iye woyendabe m'kutsutsika kwake.


pakuti ukakana kulola anthu anga amuke, taona, mawa ndidzafikitsa dzombe m'dziko lako;


Ndipo ndanena ndi iwe, Mlole mwana wanga amuke, kuti anditumikire Ine; koma wakana kumlola kuti asamuke; taona, Ine ndidzamupha mwana wako wamwamuna, mwana wako woyamba.


Ndipo pambuyo pake Mose ndi Aroni analowa nanena ndi Farao, Atero Yehova, Mulungu wa Israele, Lola anthu anga apite, kundichitira madyerero m'chipululu.


Ndipo ukakana kuwalola amuke, taona, Ine ndidzapanda dziko lako lonse ndi achule;


Ndipo Yehova anati kwa Mose, Uka nulawire mammawa, nuime pamaso pa Farao, nunene naye, Atero Yehova, Mulungu wa Ahebri, Lola anthu anga amuke, akanditumikire.


taona, dzanja la Yehova lidzakhala pa zoweta zako za kubusa, pa akavalo, pa abulu, pa ngamira, pa ng'ombe, ndi pa zoweta zazing'ono ndi kalira woopsa.


koma ngati mukana ndi kupanduka, mudzathedwa ndi lupanga; chifukwa m'kamwa mwa Yehova mwatero.


koma kwa iwo andeu, ndi osamvera choonadi, koma amvera chosalungama, adzabwezera mkwiyo ndi kuzaza,


Ndipo anatenthedwa anthu ndi kutentha kwakukulu; ndipo anachitira mwano dzina la Mulungu wokhala nao ulamuliro pa miliri iyi; ndipo sanalape kuti amchitire ulemu.