Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Eksodo 4:25 - Buku Lopatulika

Koma Zipora anatenga mpeni wamwala, nadula khungu la mwana wake, naliponya pa mapazi ake; nati, Pakuti iwe ndiwe mkwati wanga wamwazi. Ndipo Iye anamleka.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Koma Zipora anatenga mpeni wamwala, nadula khungu la mwana wake, naliponya pa mapazi ake; nati, Pakuti iwe ndiwe mkwati wanga wamwazi. Ndipo Iye anamleka.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Koma Zipora adatenga mwala wakuthwa, naumbala mwana wake, ndipo khungulo adalikhudzitsa m'miyendo mwa Mose. Kenaka Ziporayo adati, “Zoonadi, iwe ndiwe mkwati woomboledwa ndi magazi.”

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Koma Zipora anatenga mwala wakuthwa nachita mdulidwe mwana wake ndipo khungulo analikhudzitsa pa mapazi a Mose. Iye anati “Zoonadi, kwa ine ndiwe mkwati wamagazi.”

Onani mutuwo



Eksodo 4:25
6 Mawu Ofanana  

Ndipo mwamuna wosadulidwa, wosadulidwa khungu lake, munthuyo amsadze mwa anthu a mtundu wake; waphwanya pangano langa.


Ndipo anatero Simei pakutukwana, Choka, choka, munthu wa mwazi iwe, woipa iwe;


Ndipo Yetero, mpongozi wa Mose, anabwera naye Zipora mkazi wa Mose (atamtuma kwao), ndi ana ake awiri;


Ndipo Mose anavomera kukhala naye munthuyo; ndipo anampatsa Mose mwana wake wamkazi Zipora.


Pamenepo anati mkaziyo, Mkwati wamwazi iwe, chifukwa cha mdulidwe.