Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Eksodo 20:21 - Buku Lopatulika

Ndipo anthu anaima patali, koma Mose anayandikiza ku mdima waukulu kuli Mulungu.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Ndipo anthu anaima patali, koma Mose anayandikiza ku mdima waukulu kuli Mulungu.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Koma anthu ankaima kutali, Mose yekha ndiye adayandikira mtambo wamdima m'mene munali Mulungu.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Anthu aja anayima patali koma Mose anayandikira mtambo wakuda kumene kunali Mulungu.

Onani mutuwo



Eksodo 20:21
11 Mawu Ofanana  

Pamenepo Solomoni anati, Yehova ananena kuti adzakhala m'mdima waukulu.


Pamenepo Solomoni anati, Yehova anati kuti adzakhala mu mdima wandiweyani.


muvala ulemu ndi chifumu. Amene mudzikuta nako kuunika monga ndi chovala; ndi kuyala thambo ngati nsalu yotchinga.


Mwa kuchezemira kunali pamaso pake makongwa anakanganuka, matalala ndi makala amoto.


Ndipo Iye anaweramitsa thambo, natsika; ndipo pansi pa mapazi ake panali mdima bii.


Pomzinga pali mitambo ndi mdima; chilungamo ndi chiweruzo ndizo zolimbitsa mpando wake wachifumu.


Ndipo Mose anakwera kwa Mulungu; ndipo Yehova ali m'phirimo anamuitana, ndi kuti, Uzitero kwa mbumba ya Yakobo, nunene kwa ana a Israele, kuti,


Yehova ananena mau awa kwa msonkhano wanu wonse, m'phirimo ali pakati pa moto, pamtambo, pamdima bii, ndi mau aakulu; osaonjezapo kanthu. Ndipo anawalembera pa magome awiri amiyala, nandipatsa awa.


(ndinalinkuima pakati pa Yehova ndi inu muja, kukulalikirani mau a Yehova; popeza munachita mantha chifukwa cha moto, osakwera m'phirimo) ndi kuti:


amene Iye yekha ali nao moyo wosatha, wakukhala m'kuunika kosakhozeka kufikako; amene munthu sanamuone, kapena sangathe kumuona; kwa Iye kukhale ulemu ndi mphamvu yosatha. Amen.